nyatest_reg/41-MAT.usfm

2025 lines
139 KiB
Plaintext

\ide UTF-8
\h Mateyo
\toc1 Mateyo
\toc2 Mateyo
\toc3 mat
\mt Mateyo
\s5
\c 1
\cl Mutu 1
\p
\v 1 Buku ya mubadwe wa Yesu Kristu, mwana wa Davidi, mwana wa Abrahamu.
\v 2 Abrahamu anali tate wa Isaki, ndipo Isaki anali tate wa Yakobo, ndipo Yakobo anali tate wa Yuda na babale bake.
\v 3 Yuda anali tate wa Pelezi na Zela kupitila muli Tamar, Pelezi tate wa Hezeloni, ndipo Hezeloni anali tate wake wa Ramu.
\s5
\v 4 Ramu anali tate wake wa Aminadabu, Aminadabu anali tate wake wa Nashoni, and Nashoni tate wake wa Salimoni.
\v 5 Salimoni anali tate wake wa Bowazi kupitila muli Rahabu, Bowazi tate wake wa Obedi kupitila muli Lute, Obedi tate wake wa Yesse.
\v 6 Yesse anali tate wake wa Davidi mfumu, Davidi tate wake wa Solomoni kupitila mu mukazi wake wa Yuliya.
\s5
\v 7 Solomoni anali tate wake wa Rehobowamu, Rehobowamu tate wake wa Abija, Abija tate wake wa Asa.
\v 8 Asa anali tate wake wa Yehosafat, Yehosafat anali tate wake wa Yolamu, ndipo Yolamu kolo wa Uziya.
\s5
\v 9 Uziya anali tate wake wa Jotamu, Jotamu tate wake wa Ahazi, Ahazi tate wake wa Hezekaya.
\v 10 Hezekaya anali tate wake wa Manase, Manase tate wake wa Amoni, Amoni tate wake wa Josiya.
\v 11 Josiya anali kolo wa Jokoniya na abale bake pa ntawi yo pelekewa ku Babiloni.
\s5
\v 12 Kuchoka ntawi yopelekewa ku Babiloni, Yekoniya anali tate wake wa Shiyatiyewo, Shiyatiyewo anali kolo ya Zelubabewo.
\v 13 Zelubabewo anali tate wa Abiyudi, Abiyudi tate wa Eliyakimu, ndipo Eliyakimu tate wa Azo.
\v 14 Azo anali tate wa Zadoki, Zadoki tate wa Akimu, ndipo Akimu tate wa Eliyudi.
\s5
\v 15 Eliyudi anali tate wake wa Eliyaza, Eliyaza tate wa Matani, ndipo Matani tate wa Yakobo.
\v 16 Yakobo anali tate wake wa Yosefe mwamuna wa Maria, kupitila mwa eve Yesu anabadwa, wamene aitaniwa Kristu.
\v 17 Mibadwe yonse kuchokela pali Abrahamu mpaka pali Davidi inali fourteen, kuchokela pali Davidi kufikila ntawi yopelekewa ku Babiloni inali mibadwe 14, ndipo kuchokela ntawi yotengewa ukapolo ku Babiloni kufikila ntawi ya Kristu inali mibadwe 14.
\s5
\v 18 Kubadwa kwa Yesu Kristu kunachitika munjila iyi. Bamai bake, Maria, banakolobekewa kuti bakwatiliwe kuli Yosefe, koma basanabwele pamozi, banamupeza napakati kupitila muli Muzimu Oyera.
\v 19 Koma Yosefe, mwamuna wake, anali muntu olungama sanafune kuti amuchitile manyazi poonekela, mwa ichi anali kufuna kuti amusiye mwa chisinsi.
\s5
\v 20 Pamene eve anali kuganizila ivi vintu, mungelo wa Ambuye unamuonekela eve mu chiloto, nakukamba kuti, "Yosefe mwana wa Davidi, osayopa kutenga Maria kunkala mukazi wako, chifukwa eve wamene apelekewa mwa eve apelekewa na mu Muzimu Oyela.
\v 21 Azabeleka mwana mwamuna, ndipo uzamupasa zina Yesu, chifukwa azapulumusa bantu bake kuchoka kuma chimo yao."
\s5
\v 22 Ivi vonse vinachitika kuti vifikilise mau yanakambiwa na Ambuye kupitila mwa muneneli, kukamba kuti,
\v 23 "Taonani, namwali azankala na pakati na kubeleka mwana mwamuna, ndipo bazamuitana zina yake kuti Imanuweli" -yamene tantauzo yake ni, "Mulungu ali naise."
\s5
\v 24 Yosefe anauka kuchiloto chake na kucita vamene mungelo wa Ambuye unamuuza, nakumutenga kunkala mukazi wake.
\v 25 Koma sanamuzibe kufikila pamene anabeleka mwana wa mwamuna. Ndipo anamuitana zina yake kuti Yesu.
\s5
\c 2
\cl Mutu 2
\p
\v 1 Pamene Yesu anabadwa mu Betelehemu mu malo ya Yudeya mu masiku ya Helodi mfumu, bamuna bopunzila bochokela ku mawa banafika mu Yelusalemu nakukamba kuti,
\v 2 "Nanga alikuti wamene anabadwa Mfumu ya ba Yuda? Tinaona nyenyezi yake ku mawa nichifukwa chake tabwela kumupembeza."
\v 3 Pamene Helodi mfumu anamvela ichi, anavutika mutima, na Yelusalemu yonse.
\s5
\v 4 Helodi anaitanila pamozi bonse bakulu bansembe na bakalembela ba bantu, naku bafunsa kuti, "Nanga nikuti kwamene Kristu ayenela kubadwila?"
\v 5 Bana muuza kuti, "Mu muzinda wa Betelehemu kudela ya Yudeya, chifukwa ichi ndiye chamene chinalembewa na muneneli,
\v 6 'Koma iwe, Betelehemu, mumalo ya Yudeya, sindiwe ochepela pa basogoleri baku Yuda, chifukwa kuchoka kuli iwe kuzabwela olamulira wamene azasogolera bantu banga ba Israyeli.
\s5
\v 7 Koma Helodi mwachisinsi anaitana bopunzila kuti abafunse ntawi yeni yeni pamene nyenyezi inaonekela.
\v 8 Anabatuma ku Betelehemu, kukamba kuti, "Endani muka funisise mwana uyu moikako nzelu. Ngati mwamupeza, nileteleni mau mwakuti naine nibwele nimupembeze."
\s5
\v 9 Pamene banasiliza kumvela mau ya mfumu, bana enda, ndipo nyenyezi yamene banaona kumawa inabasogolela kufikila pamene inabwela yaimilila pamalo pamene panali mwana wamungóno uja analili.
\v 10 Pamene banaiona nyenyezi ija, banakondwela na chimwemwe chikulu maningi.
\s5
\v 11 Banangena munyumba nakumuona mwana mungóno anali na Maria mai wake. Banagwa pansi nakumupembeza. Bana masula tuma tumba twabo naku mupasa mpaso za golide, frankincense, na mala.
\v 12 Mulungu anaba chenjeza muchiloto kuti basabwelele kuli Helodi, chifukwa cha ichi banabwelela ku ziko yabo kusebenzesa njila inangu.
\s5
\v 13 Pamene bana enda, mungelo wa Mulungu ana onekela kuli Yosefe muchiloto naku muuza kuti, "Uka, tenga mwana mungóno na mai wake, tabila ku Igupto. Nkalani kwamene kuja kufikila pamene nizakuuza, chifukwa Helodi azasakila mwana mungóno uyu kuti amu ononge."
\v 14 Usiku wamene uja Yosefe anauka nakutenga mwana mungóno na mai wake naku enda ku Igupto.
\v 15 Anankala kwamene kuja mpaka kufikila imfa ya Helodi. Ichi china fikiliza vamene Ambuye bana kamba kupitila mumuneneli, "Kuchokela ku Igupto naita mwana wanga."
\s5
\v 16 Koma Helodi, pamene anaona kuti banamunama baja bantu bopunzila, ana kalipa maningi. Anatuma nakupaya bonse bana bamuna bamene banali mu Betelehemu na malo yonse yakuja bamene banali na zaka zibili nakubwela pansi, kukonkeleza ntawi yamene anaganizila pamene anakambisana nabopunzila.
\s5
\v 17 Ichi chinafikilisa vamene vinakambiwa kupitila muli Yelemaya muneneli.
\v 18 "Liu imveka ku Rama, kulila kwakukulu, Rakeyo ala bana bake, ndiposno akana kutontozewa, chifukwa bana bake basila."
\s5
\v 19 Pamene Helodi anamwalila, onani, mungelo wa Ambuye unaonekela muchiloto kuli Yosefe mu Igupto naku kamba kuti,
\v 20 "Uka tenga mwana na mai wake muyende ku ziko ya Israyeli, chifukwa baja bamene banali kusakila umoyo wamwana bamwalila.
\v 21 Yosefe anaima, anatenga mwana na mai wake, naku bwela ku ziko ya Israyeli.
\s5
\v 22 Koma pamene anamvela kuti Akelas anali kulamulila mu Yudeya mumalo ya tate wake Helodi, anagwiliwa na manta kuti ayendeko. Pamene Mulungu anamuchenjeza muchiloto,
\v 23 ana enda kumalo ya Galili naku yenda kukankala mu muzinda oitaniwa Nazaleti. Ichi chinafikilisa chamene chinakambiwa kupitila muli muneneli, kuti azaitaniwa mu Nazaleni.
\s5
\c 3
\cl Mutu 3
\p
\v 1 Mu ntawi ija Yohane mubatiza anabwela alalikila muchipululu cha Yudeya kuti,
\v 2 "Tembenukani, chifukwa ufumu wakumwamba uli pafupi."
\v 3 Chifukwa uyu niwamene anali kukambiwapo na Esaya muneneli, kukamba kuti, "Liu ya muntu wamene aitana muchipululu, 'Konzani njila ya Ambuye, Pangani njila yake yoyondoloka."
\s5
\v 4 Manje Yohane anavala vovala vopangiwa na usako wa Kavalo na beluti mmumazula mwake. Vakudya vake vinali ntete na uchi va musanga.
\v 5 Pamene Yelusalemu, yonse Yudeya, na malo yonse yanali kuzungulukila mumana wa Yodani bana enda kuli eve.
\v 6 Bana batiziwa kuli enve mumumana ya Yodani, bali kulapa machimo yabo.
\s5
\v 7 Koma pamene anaona ba Falisi bambili na ba Saduki bali kubwela kuli eve kuti aba batize, anabauza kuti, "Imwe bana ba njoka, nanga nindani wamene akuchenjezani kuti mutabeko ku ukali wamene ubwela?
\v 8 Balani vipaso voyenela kutembenuka.
\v 9 Osaganizila kuziuza pakati kanu kuti, 'Tilinaye Abrahamu tate watu.' Chifukwa niku uzani kuti Mulungu akwanilisa ku pasa bana Abrahamu kuchokela ku myala izi.
\s5
\v 10 Apa katemo kaikiwa kudala ku mizyu ya mitengo. Mwa ichi mutengo uli onse wamene siuzapeleka vipaso uzatemewa nakutaiwa mu mulilo.
\v 11 Nikubatizani na manzi ya kutembenuka. Koma wamene abwela pambuyo panga niwamukulu kuchila ine, koma futi na ine sindine oyenela naku nyamula nsapato zake. Azakubatizani na Muzimu Oyela na moto.
\v 12 Chokololela chake chili mumanja mwake kuti awamye malo opetelapo naku ika pamozi tiligu wake mu nkokwe. Koma azaocha vumvu zonse na moto wamene siunga zimiwe."
\s5
\v 13 Yesu anabwela kuchoka ku Galili kufika ku mumana wa Yodani kuti abatiziwe na Yohane.
\v 14 Koma Yohane anayesa yesa kuti amukanile, kukamba kuti, "Ine niyenela kuti nibatiziwe na Imwe, koma Imwe mubwela kuli ine?"
\v 15 Yesu anamuyanka nakukamba kuti, "Chivomeleze kuti chinkale njila iyi, chifukwa nicho enela kuti tifikilise ulungamo onse." Pamene apo Yohane anamu vomelesa.
\s5
\v 16 Pamene anabatiziwa, Yesu anaimilila mosachedwa kuchoka mumanzi, ndipo taonani, kumwamba kunamu segukila eve. Anaona Muzimu wa Mulungu ubwela pansi monga nkunda naku nkala pali eve.
\v 17 Onani, liu inabwela kuchokela kumwamba kukamba kuti, "Uyu ni Mwana wanga okondewa. Ndine okondwela naye maningi."
\s5
\c 4
\cl Mutu 4
\p
\v 1 Yesu anatengewa na Muzimu kuyenda mu chipululu kuti akayesewe na mudyelekezi.
\v 2 Pamene anasala chakudya muzuba na usiku masiku yokwanila 40, anamvela njala.
\v 3 Eve oyesa anabwela naku muuza kuti, "Ngati ndiwe Mwana wa Mulungu, uza izi myala kuti zisanduke kunkala mukate."
\v 4 Koma Yesu anamuyanka kuti, "chinalembewa kuti, 'Muntu sazankala na moyo kamba ka chakudya cheka, koma na mau yali yonse yamene yachokela mukamwa mwa Mulungu.'"
\s5
\v 5 Pamene apo mudyelekezi anamutenga kuyenda naye mu muzinda woyela nakumuika pa mwamba mwamba pa tempele,
\v 6 naku kumuuza kuti, "Ngati ndiwe Mwana wa Mulungu, ziponye pansi, chifukwa nicholembewa kuti, 'Eve azauza bangelo Bake kuti bakusamalile Iwe,'komanso, 'Bazakunyamula mumanja yabo, kuti usamenye kwendo Yako pa mwala.'"
\s5
\v 7 Yesu anakamba kuli eve, "Futi chinalembewa kuti, 'Usayese Ambuye Mulungu wako.'"
\v 8 Futi, mudyelekezi anamutenga pamwamba pa lupili ikulu nakumulangiza ma ufumu yonse yapa ziko yonse pamozi na ulemelelo wao.
\v 9 Anamuuza kuti, "Vonse ivi vintu nizakupasa Iwe, ngati uzagwada pansi naku nipembeza ine."
\s5
\v 10 Ndipo Yesu anamuuza kuti, "Chokapo apa iwe, Satana! Chifukwa chinalembewa kuti, 'Uzalumbila Ambuye Mulungu wako, komanso eve eka ndiye wamene muzatumikila.'"
\v 11 Pamene apo mudyelekezi anamusiya, ndipo onani, bangeli banabwela naku mutumikila.
\s5
\v 12 Manje pamene Yesu anamvela kuti Yohane anagwiliwa, anabwelela kumalo ya ku Galileya.
\v 13 Anachokako ku Nazaleti naku yenda kukankala ku Kapenamu, malo yamene yali ku nyanja ya Galileya kumalo yaku Zebuluni na Nafutali.
\s5
\v 14 Ichi chinachitika kuti vamene anakamba muneneli Yesaya vikwanilisike,
\v 15 "Malo ya Zebuluni na malo ya Nafutali, kuyangana ku nyanja, kupitilila Yodani, Galileya malo yaba Kunja!
\v 16 Bantu bamene bankala mumudima baona nchinyali chachikulu, ndiponso kuli baja bamene bankala mumalo komanso mu mfinzi ya imfa, pali beve nyali onekela."
\s5
\v 17 Kuchokela ntawi yamene ija Yesu anayamba kulalikila nakukamba kuti, "Tembenukani, chifukwa ufumu wa kumwamba wabwela pafupi."
\s5
\v 18 Pamene Yesu anali ku enda mumbali ya mumana wa Galileya, ana ona babale babili, Simoni oitaniwa kuti Petulo, na Anduru, mubale wake, banali kuponya chogwililako nsomba mu nyanja, chifukwa banali banthu wogwila nsomba.
\v 19 Yesu anakamba nabo kuti, "Bwelani, nikonkeni ine, ndipo nizakulengani kunkala bogwila babantu."
\v 20 Pamene apo banasiya vogwililako nsomba naku konka Yesu.
\s5
\v 21 Pamene Yesu anali kuyenda kuchoka kumalo uku anaona benangu babale babili, Yakobo mwana wa Zebediya, na Yohani mubale wake. Banali mu bwato na Zebediya tate wawo banali kukonza vogwililako nsomba vabo. Anabaitana,
\v 22 pamene apo banasiya bwato na batate babo naku mukonka Yesu.
\s5
\v 23 Yesu anayenda mu Galileya monse, kupunzisa mu ma Sinagogo yabo, kulalikila utenga wabwino wa ufumu, na kuchilisa matenda yosiyana siyana nakudwala pakati pa banthu.
\v 24 Utenga wa eve unayenda konse ku malo ya Siliya, ndipo bantu banamuletela bantu bonse bamene banali na matenda nakubaba kosiyana-siyana, bonse baja bamene bana tengewa na vibanda, bonse ba makate nawonse bolemala. Yesu anabachilisa.
\v 25 Magulu yakulu yanamukonka kuchokela ku malo ya Galileya, Dekapoli, Yelusalemu, na Yudeya, na konse kupitilila Yodani.
\s5
\c 5
\cl Mutu 5
\p
\v 1 Pamene Yesu anaona magulu, ana enda pa mwamba pa chulu. Pamene anankala pansi, bopunzila bake banabwela kuli eve.
\v 2 Anayamba kukamba kubapunzisa, kuti,
\v 3 "Bodalisika nibaja bosauka mumuzimu, chifukwa ufumu waku mwamba niwabo.
\v 4 Bodalisika nibaja bamene balila, chifukwa bazatontozewa.
\s5
\v 5 Bodalisika nibaja bozichepesa, chifukwa bazalandila ziko yapansi.
\v 6 Bodalisika nibaja bamane bankala na njala na njota ya chilungamo, chifukwa bazakutisiwa.
\v 7 Bodalisika nibaja bachifundo, chifukwa bazalandila chifundo.
\v 8 Bodalisika nibaja boyela mutima, chifukwa bazamuona Mulungu.
\s5
\v 9 Bodalisika nibaja bamane bapanga mutendele, chifukwa bazaitaniwa kuti nibana ba Mulungu.
\v 10 Bodalisika nibaja bamene banzunziwa chifukwa cha chilungamo, ufumu wa kumwamba niwabo.
\s5
\v 11 "Bodalisika ndiwe pamene bantu bakunyoza naku kunzunza naku kamba vosiyana-siyana voipa vaboza pali iwe chifukwa chaine.
\v 12 Kondwela ndipo nkala nachimwemwe chikulu, chifukwa malipilo yako niyakulu kumwamba. Chifukwa munjila yamene iyi beve bana nzunza baneneli bamene banali ko kumbuyo uku.
\s5
\v 13 "Ndiwe muchele wa ziko. Koma ngati muchele wasukuluka, unalengewe njila bwanji kuti unkali muchele? Ulibe ntchito iliyonse nafuti koma ku utaya panja naku dyakapo na mendo ya bantu.
\v 14 Ndimwe ku unika kwa ziko. Muzinda womangiwa pa chulu sungabisiwe.
\s5
\v 15 Kulibe bantu bamene bayasha nyali naku iika pansi pa basketi, koma pa choikapo, ndipo iunikila aliyense munyumba.
\v 16 Lekani ku unika kwanu ku onekele ku bantu munjila yakuti bangaone zintchito zanu zabwino naku peleka matamando kuli Tate wanu ali ku mwamba.
\s5
\v 17 "Musaganizile kuti ine ninabwelela ku ononga lamulo kapena baneneli. Sinina bwele ku ononga iyayi, koma kufikilisa.
\v 18 Chifukwa niku uzani kuti ngati chabe kumwamba na pansi kwa sila, kulibe ka lemba kakangóno kapena ka tito kamene kazachosewamo mu lamulo, mpaka vonse vintu vikakwanilisiwe.
\s5
\v 19 Mwa ichi ali onse wamene apwanya lamulo ingóno pali aya malamulo nakupunzisa benangu kuchita vamene ivi azaitaniwa mung'ono mu ufumu waku mwamba. Koma ali onse wamene asunga malamulo na kuya punzisa ku bena azaitaniwa mukulu mu ufumu waku mwamba.
\v 20 Niku uzani imwe kuti ngati chilungamo chanu sichizachila chilungamo cha ba kalembela naba Falisi, kulibe njila ili yonse yamene muzaka ngenelamo mu ufumu waku mwamba.
\s5
\v 21 Munamvela kuti bana uziwa bantu bakudala kuti, 'Usapaye,' futi, 'Ali onse wamene azapaya azankala muchi yopezo cha kuweluziwa.'
\v 22 Koma niku uzani imwe kuti muntu ali onse wamene ankala okalipa na mubale wake azankala muchiyopezo cha chiweluzo; koma futi ali onse wamene auza mubale wake kuti, 'iwe chimuntu ulibe pindu!' azankala muchi opezo cha ulamulilo; futi ali onse wamene akamba kuti, 'Iwe chipuba!' azankala muchi opezo cha mulilo waku gehena.
\s5
\v 23 Mwa ichi ngati upeleka chopeleka pa guwa koma wabwela wakumbukila kuti mubale wako ali na chinti kumutima chifukwa cha iwe,
\v 24 siya mpaso yako kusogolo ku guwa, enda. Choyamba bwezanani na mubale wako uja, ukasiliza ubwele upeleke mpaso yako.
\s5
\v 25 Kambisanani na wamene aku lemba mulandu mwamusanga pamene muli munjila yoyenda kuyi koti, ndaba uja okulemba mulandu azakupeleka kuli oweluza milandu, na uja oweluza milandu azaku peleka kuli musilikali, ndipo munga pelekewe mu ndende.
\v 26 Zoona niku uzani, simuzakachoka mu ndende mpaka mukalipile ndalama zonse zamene muli nazo ngonkole.
\s5
\v 27 "Munamvela kuti kunakambiwa, 'Osachite chigololo.'
\v 28 Koma niku uzani kuti bonse bamene balangana mukazi mwa chilakolako balakwa kudala na uja mukazi mu mitima zabo.
\s5
\v 29 Ngati linso yako yaku zanja lamanja ikulengesa ulakwe, ichose naku itaya. Chifukwa chawamo kuti mbali imozi ya iwe ionongeke kuchila kuti thupi yako yonse ikataiwe mu gehena.
\v 30 Ngati kwanja yako yaku dzanja lamanja iku lengesa kuti iwe ulakwe, ijube na kuitaya. Chifukwa chawamo kuti mbali imozi ya thupi yako ionongeke kuchila kuti thupi yako yonse itaiwe mu gehena.
\s5
\v 31 China kambiwa kuti, 'Ali onse wamene apisha mukazi wake, afunika kumupasa kalata yosiliza chikwati.'
\v 32 Koma nikuuzani kuti ali onse wamene asiya muzaki wake, kuchoselako mulandu wa chigololo, amulengesa kunkala wachigololo. Ali onse wamene amukwatila pamene asiyiwa na eve achita chigololo.
\s5
\v 33 "Futi, munamvela kuti chinakambiwa kuli baja bakudala kuti, 'Osalape chaboza, koma upeleke kulapa kwako kwa Ambuye.'
\v 34 Koma niku uzani, musalape nakulapa, kapena kulapila kumwamba, chifukwa ndiye kuli mupando wachifumu wa Mulungu;
\v 35 kapena ziko ya pansi, chifukwa ndiye mupando odyakapo wake; kapena Yelusalemu, chifukwa ndiye muzinda wa Mfumu ikulu.
\s5
\v 36 Kapena kulapila mutu, chifukwa sungapange sisi olo imozi yofela kapena yakuda.
\v 37 Koma lekani kukamba kwanu kunkale 'Inde, inde,' kapena 'Iyayi, iyayi.' Chili chonse chopitilila apa chichokela kuli eve oipa.
\s5
\v 38 "Munamvela kuti chinakambiwa kuti, 'Linso pa linso, koma futi lino pa lino.'
\v 39 Koma niku uzani imwe kuti, musamukane wamene ni oipa. Koma, ali onse wamene akuchayani ku mbovu imozi, mupaseni akuchayeni naku mbovu inangu iyo.
\s5
\v 40 Ngati muntu ali onse afuna kuku pelekani ku koti ndipo atenga na chovala chanu, mulekeni uyo muntu atenge na chovala cha pamwamba.
\v 41 Ali onse wamene akukakamizani kuyenda naye mutunda umozi, endani naye ibili.
\v 42 Pasani kuli ali onse wamene akupempani, ndipo musa pilikishe ali onse wamene afuna kukongola kuli imwe.
\s5
\v 43 "Munamvela kuti china kambiwa kuti, 'Uyenela kukonda neba wako naku zonda mudani wako.'
\v 44 Koma ki uzani kuti, kondani badani banu ndipo mupempelele baja bamene baku nzunzani,
\v 45 mwakuti munkale bana baba Tate banu bamene bali kumwamba. Chifukwa beve bama lenga zuba ku sanika pali baja boipa nabaja babwino, naku tuma mvula pali baja bolungama nabaja bosalungama.
\s5
\v 46 Chifukwa ngati iwe ukonda chabe baja bamene bakukonda, upezamo chani? Nanga simwamene baja bamusonko bamachitila?
\v 47 Ngati mupasa moni chabe babale bane, kansi kusiyana kwanu nabaja benangu kuli pati? Simwamene ba Kunja bamachitila?
\v 48 Mwa ichi imwe muyenela kunkala bolungama, monga mwamene balili ba Tate banu baku mwamba.
\s5
\c 6
\cl Mutu 6
\p
\v 1 "Onesesani kuti simuchita nthito zanu za chilungamo pa menso pa bantu kuti baku oneni, chifukwa simuzalandila malipilo kuchokela kuli ba Tate banu bamene bali kumwamba.
\v 2 Pamene mupeleka thandizo, musalinze lipenga monga mwamene baboza bamachitila muma Sinagogo na munjila, mwakuti bangalandile matamando yochoka kuli bantu. Zo ona niku uzani, balandila malipilo yabo.
\s5
\v 3 Koma pamene mupeleka thandizo, musaleke kwanja yanu ya kwanja ya manzele izibe chamene kwanja ya manja ichita
\v 4 mwakuti mpaso yanu ipelekewe posaonekela. Mwa ichi Tate wanu wamene ali mobisika azakupasani malipilo.
\s5
\v 5 "Pamene mupempela, musankale monga baja ba boza, chifukwa bama konda kuimilila muma Sinagogo na muma kona mwa njila kuti baonekele ku bantu. Zo ona niku uzani imwe, balandila malipilo yabo.
\v 6 Koma imwe, pamene mupempela, endani muchipinda chamu kati. Valani chiseko mupempele kuli ba Tate banu, Bamene bali mobisika. Ba Tate banu bamene baona mu chisinsi bazakupasani malipilo.
\v 7 Pamene mupempela, musa kambe mobwezapo bwezapo vilibe na pindu monga ba Kunja mwamene bachitila, chifukwa baganiza kuti bazaba mvela chifukwa cha kupaka kwa mau yabo mu pempelo.
\s5
\v 8 Mwa ichi, musankale monga beve, chifukwa ba Tate banu baziba vamene imwe mufuna mukalibe naku pempa.
\v 9 Mwa ichi pempelani munjila iyi: 'Ba Tate batu bamene muli kumwamba, lekani zina yanu ilemekezeke monga yoyela.
\v 10 Lekani ufumu wanu ubwele. Lekani kufuna kwanu kuchitike pa ziko monga mwamene chilili kumwamba.
\s5
\v 11 Mutipase lelo mukate watu walelo.
\v 12 Tikululukileni ma chimo yatu, monga mwamene ise tikululukila bamene bati lakwila ise.
\v 13 Musatipeleke mu ma yeso, koma mutichose ku oipa.'
\s5
\v 14 Chifukwa ngati imwe mukululukila bantu volakwa vabo, ba Tate banu baku mwamba baza kukululukilani naimwe.
\v 15 Koma ngati imwe simukululukila volakwa vabo, naimwe ba Tate banu sibazakukululukilani volakwa vanu.
\s5
\v 16 "Pamene muzimana chakudya, musankale na pamenso monga mulila monga mwamene bantu baboza bamachitila, chifukwa bama chinja pamenso kuti baonekele ku bantu kuti ba zimana chakudya. Zo ona ni kuuzani imwe, balandila malipilo yabo.
\v 17 Koma imwe, pamene muzimana chakudya, zolani mafuta ku mutu musambe na ku menso
\v 18 kuti musaonekele kuli bantu kuti muzimana chakudya, koma kuli ba Tate banu chabe bamene bali mobisika; ba Tate banu bamene baona mobisika bazakupasani malipilo.
\s5
\v 19 "Musazisungile mweka chuma pa ziko, pamene vidoyo na nguwe imaononga, futi pamene ba kawalala bama ngena naku ba.
\v 20 Koma, zisungileni mweka chuma kumwamba, kwamene vidoyo kapena nguwe si ingaononge, kwamene ba kawalala siba ngangene na kuba.
\v 21 Chifukwa kwamene kuli chuma yanu, kwamene uko ndiye kuzankala na mutima wanu.
\s5
\v 22 Linso ndiye nyali ya ku thupi. Mwa ichi, ngati linso yanu ili bwino, thupi yanu yonse izankala yozula na ku ngwelebela.
\v 23 Koma ngati linso yanu niyo ipa, thupi yanu yonse izankala na mudima. Mwa ichi, ngati nyali yanu yamene ili mukati mwanu ni mfinzi, onani kukula kwa chimudima icho!
\v 24 Kulibe kapolo angasebenzele ba kazembe babili, chifukwa aza zondapo umozi naku konda uja winangu, kapena azazipeleka kuli umozi na kunyozela uja winangu. Simunga tumikile Mulungu na chuma.
\s5
\v 25 Mwa ichi ni kuuzani imwe, musankale ovutika pa zau moyo, vamene muzadya kapena vamene muzamwa; kapena pa za thupi, vamene muzavala. Kansi moyo siuchila vakudya, na thupi si ichila vovala?
\v 26 Onani tunyoni twa mumwamba. Situmalima kapena kukolola kuika mu nkokwe, koma Tate wanu waku mwamba amatudyesa. Nanga imwe sindimwe ba mutengo wapa mwamba kuchila tweve?
\s5
\v 27 Nindani pali imwe wamene muku pitila movutikila mutima angaikileko ku utali wa umoyo wake?
\v 28 Nanga nichifukwa chani muvutika mutima pali vovala? Ganizilaniponi pali tuma luwa twa mu sanga, mwamene tuma kulila. Situma sebenza, situmatunga vovala.
\v 29 Koma niku uzani imwee kuti, Solomo mu ulemelelo wake onse sana valeko monga tuma luba utu.
\s5
\v 30 Ngati Mulungu amavalika ma uzu sanga, yamene lelo yaliko koma mailo yataiwa mu mulilo, kuchilapo njila bwanji mwamene Mulungu azaku valikani imwe, imwe bochepekela chikululupilo?
\v 31 Mwa ichi musankale bovutika mutima nakukamba kuti, 'nanga tizadya chani kansi' kapena 'Nanga tizamwa chani kansi?' kapena 'Nanga tizavala vovala viti kansi?'
\s5
\v 32 Chifukwa bakunja bamafunafuna ivi vintu, koma ba Tate banu baziba kuti mufunikila ivi vintu.
\v 33 Koma choyamba funani ufumu waku mwamba na chilungamo chake, ndipo ivi vonse muzapasiwa.
\v 34 Mwa ichi, musankale bovutika mutima pa za mailo, chifukwa mailo iza zivutikila pa yka. Siku iliyonse ilinavo voipa vake yeka.
\s5
\c 7
\cl Mutu 7
\p
\v 1 Osaweluza, naiwe siuzaweluziwa.
\v 2 Chifukwa mwamene iwe uweluzila benangu ndiye mwamene naiwe uzaweluziwa, na mwamene uzapimila chiweluzo chako ndiye mwamene bazakuweluzila naiwe.
\s5
\v 3 Nanga nichani ulanganila pa kauzu kamene kali mu linso ya mubale wako koma uibala chi nkuni chamene chili mu linso yako?
\v 4 Nanga uzamuuza bwanji mubale wako kuti, 'Leka nikuchose ka uzu kali mu linso yako,' koma chinkuni chili mu linso yako?
\v 5 Iwe wa boza! Yambilila kuchosa chinkuni mu linso yako, kuchoka apo ndiye pamene uzaona bwino kuti ukwanisa kuchosa kauzu kali muli linso ya mubale wako.
\s5
\v 6 Osapasa imbwa vintu voyela, ndipo musaponyele myala zamutengo wapatali pamenso pa nkumba ya musanga. Ndaba vizadyakapo na mendo, nakupindamuka naku kusansaulani imwe.
\s5
\v 7 "Pempa, ndipo uzapasiwa. Sakila, ndipo uzapeza. Konkosha, ndipo bazakusegulila.
\v 8 Chifukwa muntu aliwonse wamene apempa amalandila; aliwonse wamene amasakila, amapeza; na kuli uja wamene akonkosha, bazamusegulila.
\v 9 Kaya ngati nindani pali imwe, wamene ngati mwana wake amupempa buledi, azamupasa mwala?
\v 10 Kapena ngati apempa nsomba, azamupasa njoka?
\s5
\v 11 Mwa ichi, ngati imwe boipa muziba kupasa mpaso zabwino kuli bana banu, nanga ba Tate banu bali kumwamba bazakuchitilani bwanji mukupasa vintu vabwino kuli baja bamene baba pempa?
\v 12 Mwa ichi, chilichonse chamene ufuna kuti bantu bakuchitile iwe, naiwe uyenela kubachitila, aya ndiye ma lamulo na baneneli.
\s5
\v 13 Ngena kupitila pa chiseko chingóno. Chifukwa chiseko na njila ikulu ndiye vamene vipeleka ku chionongeko, ndiponso nibambili bamene ba ngenela mwamene umo.
\v 14 Koma chiseko nichingóno na njila niyovuta yamene ipeleka kuli moyo, ndipo nibangóno bamene baipeza.
\s5
\v 15 Nkalani bochenjela naba neneli baboza, bamene babwela kuli imwe bavala vovala va nkosa koma mukati ni mimbulu yanjala ikulu.
\v 16 Muzabazibila kuvipaso vabo. Nanga bantu bamatyola mpesa ku mutengo waminga kapena mukuyu ku minga?
\v 17 Munjila imozi-mozi, mutengo onse wabwino umabala vipaso vabwino, koma mutengo oipa umabala vipaso voipa.
\s5
\v 18 Mutengo wabwino siungabale vipaso voipa, kapena mutengo oipa kubala vipaso vabwino.
\v 19 Mutengo uli onse wamene siumabala vipaso vabwino umatyolewa naku taiwa mu mulilo.
\v 20 Mwa ichi, muzabaziba kupitila muvipaso vabo.
\s5
\v 21 Simuntu aliwonse wamene akamba kuli ine kuti, 'Ambuye, Ambuye,' wamene azakangena mu ufumu wakumwamba, koma baja chabe bamene bachita chifunilo chaba Tate banga bamene bali kumwamba.
\v 22 Bambili bazakamba kuli ine pa siku ija, 'Ambuye, Ambuye, ife sitinali kupeleka uneneli mu zina yanu, muzina yanu tinali kuchosa vibanda, muzina yanu tinachita vintu vikulu kwambili?
\v 23 Pamene apa nizakabauza po onekela kuti, 'Sininakuzibeni! Chokani pamenso panga, imwe bamachitidwe yoipa!'
\s5
\v 24 "Mwaichi, muntu aliwonse wamene amvela mau yanga na kuchita vamene nakamba azankala monga muntu wamene amanga nyumba yake pa mwala.
\v 25 Mvula inagwa, vimanzi vinabwela, na chimpepo chinaputa na kumenya nyumba ija, koma si inagwe pansi, chifukwa ina mangiwa pa mwala.
\s5
\v 26 Koma muntu aliwonse wamene amvela mau yanga koma sachita vamene nakamba ali monga uja muntu opusa wamene anamanga nyumba yake pa muchenga.
\v 27 Mvula inagwa, vimanzi vinabwela, na chimpepo chinaputa na kumenya ija nyumba, ndipo inagwa, na kuonongeka kwake kunali kuja kofikapo.
\s5
\v 28 Pamene Yesu anasiliza kukamba aya mau, magulu ya bantu yanadabwa na kupunzisa kwake,
\v 29 chifukwa anali kubapunzisa monga uja muntu wamene ali na ulamulilo, osati monga baja bakalembela.
\s5
\c 8
\cl Mutu 8
\p
\v 1 Pamene Yesu anaseluka ku pili, magulu ya bantu yanamukonka.
\v 2 Onani, muntu wa makate anamukonka na kugwada pansi, nakukamba kuti, " Ambuye, ngati mufuna, mungani polese."
\v 3 Yesu anatambasula kwanja yake naku mugwila, naku kamba kuti, " Nifuna. Pola." Pamene apo eve anapolesewa ku matenda yake ya makate.
\s5
\v 4 Yesu anamuuza kuti, " Onesesa kuti usauze muntu aliwonse kantu. Yenda, kazilangize kuli mukulu wa nsembe, na kupeleka chopeleka chamene Mose anakuuzani, kupeleka umboni kuli beve."
\s5
\v 5 Pamene anali kubwela ku Kapenamu, mukulu wabasilikali anabwela kuli eve, kumupempa
\v 6 nakukamba kuti, "Ambuye, wantchito wanga kunyumba aligone adwala alibe mpavu ndipo amvela kubaba kukulu."
\v 7 Pamene apo Yesu anamuuza kuti, " Nizabwela nimupolese."
\s5
\v 8 Eve mukulu wa asilikali anamuyanka nakuti, "Ambuye, ine sindine oyenela kuti imwe mubwele kungenda munyumba yanga. Koma kambani chabe mau wantchito wang aazapola.
\v 9 Chifukwa ine ndine muntu wamene ali pansi pa bakulu bantchito, naine nilinabo basilikali pansi panga. Nikamuuza umozi kuti, 'yenda,' amayenda, nakuli winangu kuti, 'bwela,' amabwela, nakuli wantchito wanga kuti, 'Chita ichi,' amachita."
\v 10 Pamene Yesu anamvela ivi, anadabwa nakuuza bantu bamene banali kumukonka kuti, "Zoona nikuuzani imwe, nikalibe kupezapo muntu aliwonse wamene ali na chikulupililo monga ichi mu Israeli.
\s5
\v 11 Nikuuzani kuti, bantu bambili bazakabwela kuchokela kumawa na ku mazulo, ndipo bazankala pamalo podyela pamozi na Abrahamu, Isaki, na Yakobo, mu ufumu wakumwamba.
\v 12 Koma bana ba mu ufumu bazataiwa panja mumu mudima, kwamene kuzankala kulila na kusheta meno."
\v 13 Yesu anakamba kuli uja mukulu waba silikali, "Yenda! Monga mwamene wakulupilila, leka chikuchitikile iwe." Uja wantchito wake anapolesewa pa ntawi yamene ija.
\s5
\v 14 Pamene Yesu anabwela munyumba ya Petulo, anaona bapongozi ba Petulo baligone namatenda ya kupya tupi.
\v 15 Yesu anagwila kwanja yabo, kupya tupi kunayenda pamene apo. Banaima na nakuyamba kumusebenzela.
\s5
\v 16 Pamene kunankala ntawi yaku mazulo, bantu banaleta kuli Yesu bantu bambili bamene banali na zibanda. Anabachosa vibanda kusebenzesa chabe mau nakupolesa bonse bamene banali namatenda.
\v 17 Munjila iyi mau yamene yanakambiwa na muneneli Yesaya yanafikilisiwa, kukamba kuti, "Eve eka anatitengela kusamvela bwino kwatu naku nyamula matenda yatu."
\s5
\v 18 Manje pamene Yesu anaona gulu yabantu banamuzungulukila anabauza kuti bachokeko bayenda kumbali ina ya Galili.
\v 19 Ndipo eve wolemba anabwela kuli Yesu nakukamba kuti, "Mupunzisi, ine nizakukonkani kuli konse kwamene imwe muzayenda."
\v 20 Yesu anamuuza kuti, "Nkandwe zili na monkala, tunyoni twa mumwamba tuli nato tuchisa, koma Mwana wa muntu eve alibe na poika mutu."
\s5
\v 21 Wina pali wopunzila anamuyanka kuti, "Ambuye, nivomeleseni kuti niyende nikashike ba tate banga."
\v 22 Koma Yesu anamuuza kuti, "Konka ine, baleke bakufa bashikane beka."
\s5
\v 23 Pamene Yesu anangena mu bwato, bopunzila bake banamukonka.
\v 24 Onani, kunabwela chimpepo chikulu pa nyanja, mwakuti bwato inazula na manzi. Koma Yesu anali akali gone.
\v 25 Bopunzila bake banenda kuli eve na kumuusha, nakumuuza kuti, "Tipulumuseni, Ambuye; tifuna kufa!
\s5
\v 26 Yesu anakamba kuli beve kuti, "Nanga nichani muli na manta, imwe bochepa chikulupililo?" Anaima naku kalipila chipempo na nyanja. Chipempo chinabwela chasila.
\v 27 Bantu baja banadabwa kwambili nakukamba kuti, "Nanga nimuntu wa bwanji kansi uyu, wamene na chimpepo na nyanja vimumvelela?"
\s5
\v 28 Pamene Yesu anabwela kumalo kwina ku ziko yaku ba Gadalene, bamuna babili bamene banali na vibanda banamukumanya eve. Banali kuchokela ku manda ndipo banali ba ndeo, chifukwa chake kulibe muntu wamene anali pa ulendo wamene anali kupitila njila iyi.
\v 29 Onani, banapunda nakukamba kuti, "Nanga nichani chamene ufuna kuli ise iwe, Mwana wa Mulungu? Nanga wabwela kuno kuti utizunzise pamene ntawi yamene inaikiwa ikalibe kufika?"
\s5
\v 30 Manje gulu ya nkumba inali kudya, osati kutali maningi na beve. Vibanda vinapitiliza kumupempa Yesu kuti,
\v 31 "Ngati mwatichosa, tiuzeni tiyenda muli gulu ya nkumba."
\v 32 Yesu anaviuuza kuti, "yendani!" Vibanda vinachoka nakuyenda mu nkumba; ndipo onani, gulu yonse ya nkumba zinataba nakuyenda kuseluka chulu kuyenda mu nyanja mwamene zinafela mumanzi.
\s5
\v 33 Baja bamene banali ku betela nkumba banataba naku enda mu muzinda naku uza bantu vonse vamene vinachitika, maka-maka vamene vinachitika kuli baja bamene banali na vibanda.
\v 34 Onani, muzinda onse unabwela kuti uone Yesu. Pamene banamu ona Yesu, banamupapatila kumupempa kuti achoke ku malo yabo.
\s5
\c 9
\cl Mutu 9
\p
\v 1 Yesu anangena mu bwato, naku enda kumbali kwina kwa nyanja, nakufika ku muzinda kwake.
\v 2 Onani, banamuletela muntu wama manjenje aligone pa mpasa. Pamene anaona chikulupililo chabo, Yesu anamu uza uja muntu, "Mwana, nkala okondwela. Machimo yako yakululukiwa."
\s5
\v 3 Onani, benangu pali bolemba banayamba kukamba pabeka kuti, "Uyu muntu anyoza."
\v 4 Yesu anaziba maganizo yabo naku bauza kuti, "Nanga nichani imwe muganiza voipa mumitima zanu?
\v 5 Nanga nichiti chintu chamene sichishupa, kukamba kuti, 'Machimo yako yakululukiwa,' kapena kukamba kuti, 'Ima uyende'?
\v 6 Koma kuti imwe muzibe kuti Mwana wa Muntu alinayo mpavu pa ziko yo kululukila machimo, ... anakamba ku uza uja wamanjenje kuti, "Imilila, tenga mpasa yako, enda kunyumba kwako."
\s5
\v 7 Pamene apo mwamuna uja ananyamuka naku enda kunyumba kwake.
\v 8 Pamene gulu ya bangtu inaona ivi, banadabwa nakuyamba kutamanda Mulungu, wamene anapasa mpavu zamutundu uyu ku bantu.
\v 9 Pamene Yesu anali kupita paja, anaona muntu zina yake Mateyo ali nkale posebenzela baja bamusonko. Anamu uza eve kuti, "Nikonke." Anaima nakumukonka.
\s5
\v 10 Pamene Yesu anankala kuti adye munyumba, onani, bambili ba musonko na bamachimo banabwela nakudya pamozi na Yesu na bopunzila bake.
\v 11 Pamene ba Falisi banaona ivi, banakamba kuli bopunzila ba Yesu kuti, "Nanga kansi nichani chamene bapunzinsi banu badyela pamozi naba musonko na bantu bama chimo?
\s5
\v 12 Pamene Yesu anamvel aivi, anakamba kuti, "Bantu bamene bali bwino mu mubili sibafunika kuona dotolo, koma baja bamene nibodwala.
\v 13 Endani muka punzile tantauzo ya kukamba uku: 'Ine nifunapo kunkala na chifundo kuchilapo nsembe.' Chifukwa ine sininabwele kuitana bolungama kuti batembenuke, koma bamachimo.
\s5
\v 14 Bopunzila ba Yohane banabwela kuli eve nakukamba kuti, "Nanga nichani ise na ba Falisi timazi mana chakudya kambili, koma bopunzila banu beve sibama zimana?"
\v 15 Yesu anaba yanka, "Nanga bantu boitaniwa ku ukwati banga mvese chifundo pamene okwatiliwa akali nabo? Koma ma siku yazakabwela pamene okwatiliwa azakatengewa, pamene apo bazakazimana chakudya.
\s5
\v 16 Kulibe muntu wamene aika kanyula ka manje pali chovala chakudala, chifukwa kanyul aaka kazangámba chovala, kungámbika kweve kuzankala kukulu.
\s5
\v 17 Nafuti bantu sibamaika vinyo va manje mu voikamo vakudala. Ngati bachita ichi, voikamo vizapwanyika, vinyu vizataika, na voikamo vizaonongeka. Koma, bamaika vinyu va manje mu voikamo vamanje, munjila iyi vonse visasungiwa chabe bwino.
\s5
\v 18 Pamene Yesu anali kubauza ivi vintu, onani, kazembe umozi anabwela naku gwada kuli Yesu. Nakukamba kuti, "Mwana wanga mukazi amwalila, koma bwelani mumuike kwanja, azauka."
\v 19 Pamene apo Yesu anaima naku mukonka, na bopunzila bake na beve banakonka.
\s5
\v 20 Onani, mukazi wamene anali na vuto yochoka magazi zaka zopitilila kumi ya zibili anabwela kumbuyo kwa Yesu naku gwila kunyansi ya chovala chake.
\v 21 Chifukwa anaziuza mukazi uyu eka kuti, "Ngati chabe nagwila vovala vake, Ine nizankala chabe bwino."
\v 22 Koma Yesu anapindimuka naku muona, nakukamba kuti, "Mwana wanga mukazi, nkala olimba, kukulupilila kwako kwaku polesa." Pamene apo uja mukazi anapola.
\s5
\v 23 Pamene Yesu anafika munyumba ya uja kazembe, anaona bolinza mitoli na gulu ya bantu ipanga chongo.
\v 24 Anabauza kuti, "Tiyeni endani, uyu mukazi sanamwalile, koma agona chabe." Koma banamu seka monyezela.
\s5
\v 25 Pamene gulu ija inachoka panja, anangena mu chipinda naku mugwila kukwanja, mukazi uja anauka.
\v 26 Nkani ya uyu utenga ina enda mumalo yonse.
\s5
\v 27 Pamene Yesu anali kupita kuchokela kuja, bamuna babili bamen banalibe menso banamukonka. Banapitiliza kupunda naku kamba kuti, "Tichitileni chifundo ise, Mwana wa Davide!"
\v 28 Pamene Yesu ananegna munyumba, bamuna baja banalibe menso banabwela kuli eve. Yesu anabauza kuti, "Mukulupilila kuti ninga kwanise ichi?" Bana muyanka kuti, "Inde, Ambuye."
\s5
\v 29 Pamene apo Yesu anabagwila pamenso nakukamba kuti, "Lekani chikuchitikileni kulingana na chikulupililo chanu,"
\v 30 na menso yabo yanaona. Yesu anabauza mobalimbikisa kuti, "Onani kuti kulibe muntu ali onse wamene azaziba ichi."
\v 31 Koma bamina baja babili bana enda naku peleka mau ku malo yonse yakuja.
\s5
\v 32 Pamene baja bamuna banali kuenda, onani, mwamuna chiulu wamene anali na vibanda banamuleta kuli Yesu.
\v 33 Pamene chibanda chinachosewa, uja chibulu anayamba kukamba. Ma gulu ya bantu yana dabwa nakukamba kuti, "Ichi chikalibe kuonekapo mu Islayeli!"
\v 34 Koma ba Falisi beve banali kukamba kuti, "Nichifukwa cha mukulu wa vibanda, ndiye chamene akwanilisila kuchosa vibanda."
\s5
\v 35 Yesu anaenda-enda mumizinda na muminzi yonse. Anapitiliza kupunzisa muma sinagogo yabo, kulalika utenga wa ufumu na kupolesa matenda yamu tundu onse na kusamvela bwino kosiyana-siyana.
\v 36 Pamene anaona magulu, anamvela chifundo, chifukwa banali bovutika mitima nafuti bobwezewa kumbuyo. Banali monga nkosa zamene zilibe ozibeta.
\s5
\v 37 Anakamba kuli bopunzila bake kuti, "Vokolola nivambili, koma banchito ndiye bamene bachepa.
\v 38 Chifukwa chake imwe muyenela kupempela kuli Ambuye ba vokolola, kuti batume banchito mu munda wabo."
\s5
\c 10
\cl Mutu 10
\p
\v 1 Yesu anaitana bopunzila bake nakubapasa mpavu pali mizimu za doti, kuti bazivichosa, naku polesa matenda yosiyana-siyana na kusamvela bwino kuli konse.
\s5
\v 2 Mazina ya bopunzila bali kumi imozi na tubili ni aya. Oyamba, Simoni (wamene anapasa zina yakuti Petulo), na Andulu mubale wake; Yakobo mwana wa Zebedi, na Yohane mubale wake;
\v 3 Filipi, na Batolomeu; Tomasi, na Mateyo uja wamusonko; Yakobo mwana wa Alufeyo, na Tadeyasi;
\v 4 Simoni Siloti, na Yudasi Isikalioti, wamene anamugulisa.
\s5
\v 5 Aba bali kumi na tubili Yesu anabatuma. Anabapasa lamulo nakubauza kuti, "Musangene mumalo yali yonse kwamene kunkala ba Kunja, nafuti musangene mu muzina uli onse waba Samalita.
\v 6 Koma endani kuli nkosa zotaika za munyumba mwa Islayeli,
\v 7 pamene mu enda, mukazilalikila nakukamba kuti, 'Ufumu waku mwamba wabwela pafupi.'
\s5
\v 8 Polesani bodwala, ukisani bantu bakufa, polesani bali na makate, chosani vibanda. Mwalandila mosalipila, naimwe pasani mosalipilisa.
\v 9 Musatenge golide ili yonse, siliva, kapena kopa mu ma tumba yanu.
\v 10 Musatenge chola pa ulendo wanu, kapena chovala chinangu, kapena nsapato, kapena ndodo, chifukwa wantchito ayenekela kumupasa chakudya.
\s5
\v 11 Muzinda uli onse kapena munzi uli onse wamene mwangenamo, pezani wamene ali onela mwamene umo, nkalani mwamene umo mpaka mukachokemo.
\v 12 Pamene mungena munyumba iyo, pelekani moni.
\v 13 Ngati nyumba niyoyenela, lekani mutendele wanu unkale pali yeve. Koma ngati siyoyenela, lekani mutendele wanu ubwelele kuli imwe.
\s5
\v 14 Koma kuli baja bamene sibakulandilani kapena kumvela mau yanu, pamene imwe muchoka munyumba ija kapenam muzinda, chosani doti kumendo yanu.
\v 15 Niku uzani cha zo-ona kuti, chizainkalilako bwino malo ya Sodoma na Gomola pa siku yoweluza kuchilapo muzinda uyo.
\s5
\v 16 "Onani, Nikutumani monga nkosa pakati pa mimbulu, chifukwa chake nkalani bochenjela monga njoka koma na mutima monga wa nkunda.
\v 17 Koma nkalani bochenjela na bantu! Bazakupelekani kuli bakulu ba milandu, ndipo bazakumenyani mu ma sinagogo yabo.
\v 18 Kukonkapo bazakuletani pa menso pa ba Kazembe na mafumu chifukwa cha Ine, kunkala monga mboni kuli beve na kuli bakunja.
\s5
\v 19 Pamene bakupelekani, musankale bovutika mutima pali mwamene muzakambila kapena vamene muzakamba, chifukwa vamene muzafunika kukamba pali ntawi yamene ija muzakapasiwa.
\v 20 Chifukwa sindimwe bamene muzakamba iyayi, koma Muzimu wa Atate banu ndiye wamene azakamba kupitila muli imwe.
\s5
\v 21 Mubale azakapeleka mubale wake ku imfa, na tate mwana wake. Bana bazaka ukila makolo yabo nakulengesa kuti babapaye.
\v 22 Muzazondewa na bonse chifukwa cha zina yanga. Koma wamene azakalimbikila kufikila kosilizila, uja munt azakapulumuka.
\v 23 Pamene bazaku vutisani mumuzinda uyu, tabilani ku muzinda winangu, chifukwa niku uzani imwe, simuzaka kwanisa kuyendamo mumizinda za Islayeli zonse Mwana wa Muntu akalibe naku bwela.
\s5
\v 24 "Opunzila simukulu kuchila omupunzisa, kapena wanthito achile bwana wake.
\v 25 Chilibwino kuti opunzila ankale monga omupunzisa, na wanchito ankale monga bwana wake. Ngati bana itana bwana wa nyumba kuti eve ni Belezebabu, nanga bantu bamu nyumba bake bazaba itana mazina yoipapo bwanji kansi!
\s5
\v 26 Chifukwa chake imwe musaba yope, chifukwa kulibe kantu kamene nikobisika kamene sikazakaonesewa, nafuti kulibe kamene kali nikobisika kamene sikazazibika.
\v 27 Vamene niku uzani usiku, vikambeni muzuba, na vamene mumvela mobweza mau mu matu, vikambeni pa mwamba pa mutenge.
\s5
\v 28 Mosayopa baja bamene bapaya tupi koma sibakwanisa kupaya moyo. Koma, yopani wamene akwanisa kuononga moyo na tupi ku nganjo ya moto.
\v 29 Nanga kansi tu nyoni tubili situma gulisiwa pa ka ndalama kamozi? Koma kulibe nangu kamozi kamene kamagwa pansi Atate banu osaziba.
\v 30 Koma naimwe sisi zanu mumutu zonse nizopendewa.
\v 31 Musayope. Imwe ndimwe bamutengo wapatali kuchila tunyoni twambili.
\s5
\v 32 Chifukwa cha ichi muntu ali onse wamene anivomela pamenso pa ya bantu, naine nizamu vomela pammenso ya Atate banga bamene bali kumwamba.
\v 33 Koma uja wamene anikana pamenso ya bantu, naine nizakamukana pamenso yaba Tate banga bamene bali kumwamba.
\s5
\v 34 "Musaganize kuti ine ninabwela kuleta mutendele pa ziko yapansi. Sininabwelele kuleta mutendele, koma lupanga.
\v 35 Chifukwa ine ninabwela kuika mwamuna kushushana na tate wake, mwana mukazi kushushana na mai wake, na mupongozi mukazi kushushana na bapongozi bakazi bake.
\v 36 Bozonda muntu bazankala bamene baja bamu nyumba yake.
\s5
\v 37 Uja wamene akonda batate bake kapena bamai bake kuchila ine sayenela ine; wamene akonda mwana mwamuna kapena mwana mukazi kuchila ine sioyenela ine.
\v 38 Wamene sazanyamula mutanda wake nakuni konka ine sayenela ine.
\v 39 Wamene apeza moyo wake azautaya. Koma wamene ataya moyo wake chifukwa cha ine azaupeza.
\s5
\v 40 Wamene akulandilani imwe alandila ine, na uja wamene alandila ine alandila eve wamene ananituma.
\v 41 Wamene alandila muneneli chifukwa ni muneneli azalandila malipilo ya muneneli, na uja wamene alandila muntu wachilungamo chifukwa ni olungama azalandila malipilo ya muntu olungama.
\s5
\v 42 Ali onse wamene apasa olo chabe manzi yakumwa yozizila kuti amwe mwana wamene ali opunzila wanga, zo-ona niku uzani imwe, sazataya malipilo yake."
\s5
\c 11
\cl Mutu 11
\p
\v 1 Pamene Yesu anasiliza ku uza bopunzila bake bali 12 vochita, anachokako kuyenda mukupunzisa mumizinda zabo naku lalikila.
\v 2 Manje pamene Yohane anamvela pali vamene Kristu anali kuchita, anatumiza mau kupitila muli bopunzila bake
\v 3 kukamba kuti, "Kansi ndiwe wamene ubwela, kapena nangu tiyembekeze winangu?"
\s5
\v 4 Yesu anabayanka nakukamba kuti, "Yendani mukamuuze Yohane vamene muona navamene munvela.
\v 5 Mpofu ziona, bolemala mendo bayenda, bamakate bapola, ba chiulu bamvela futi, bakufa baukisiwa nafuti, na utenga ulalikiliwa kuli baja bosauka.
\v 6 Odalisika niuja wamene sakalipa chifukwa cha ine."
\s5
\v 7 Pamene aba bantu banali kuyenda pa ntchito yabo, Yesu anayamba kuuza magulu pali Yohane kuti, "Nanga kansi mwenze munayenda kuona chani muchipululu-ka uzu konyangányisiwa na chipempo?
\v 8 Nanga nichani chamene mwenze mwayenda kuona kansi-muntu wamene avala vovala vabwino? Zoona, baja bamene bavala vovala vabwino bankala mu manyumba ya ufumu.
\s5
\v 9 Kansi mwenze mwa enda kuona chani-muneneli? Zoona, nikuuzani imwe, koma futi kuchilapo napali muneneli chabe.
\v 10 Uyu ndiye wamene vinalembewapo vokamba kuti, 'Ona, nizatuma wautenga wanga pamenso yanu, wamene azakukonzelani njila.'
\s5
\v 11 Nikamba kuli imwe chazoona, pali bonse wobadwa kuli bakazi kulibe mukulu ochila Yohane Mubatizi. Koma uja wochepa mu ulemelelo mu ufumu waku mwamba amuchila uyu.
\v 12 Kuyambila masiku ya Yohane Mubatizi kufikila apa mamnje, ufumu wakumwamba wavutika na pokoso, na baja bapokoso bautenga mwa mpavu.
\s5
\v 13 Chifukwa bonse baneneli na malamulo yanali kunenela kufikila mpaka Yohane;
\v 14 ngati ndimwe bokonzekela kuchivomela ichi, uyu ndiye Eliya wamene anali kubwela.
\v 15 Wamene ali na matu yamene yamvela, mulekeni amvele.
\s5
\v 16 Kansi uyu mubadwe ninga ulinganisane na chani? Uli monga bana bamene basobela pa malo yama londa, bamene bankala nakuitanana wina na munzake
\v 17 naku kamba kuti, 'Takulinzila mutolilo iwe, koma iwe sunavine. Talila, koma iwe sunalileko.'
\s5
\v 18 Chifukwa Yohane sanabwele akudya kapena na kumwa vinyu, koma bakamba kuti, 'ali na chibanda.'
\v 19 Mwana wa Muntu anabwela akudya na kumwa bakamba kuti, 'Onani, nikamukonda kudya nafuti ni chakolwa, munzake waba musonko na bantu bamachimo!' Koma nzelu zima weluzika zolungama kulangana zna ntchito ake"
\s5
\v 20 Yesu anayamba kukalipila mizinda mwamene ntchito zake zikulu zinachitikiliwa, chifukwa sibama tembenuke.
\v 21 "Soka kuli iwe, Kolazini! Soka kuli iwe, Betisaida! Chifukwa ngati ncthito zamene zachitika mukati mwanu asembe zinachitikiliwa mu Tayala na mu Sidoni, asembe banatembenuka kudala bali vale na vovala vama saka na milota.
\v 22 Koma chozabankalilako bwino baku Tayala na Sidoni pa siku ya chiweluzo kuchila imwe.
\s5
\v 23 Iwe, Kapenamu, uganiza monga uzakwezewa kumwamba? Iyayi, uzaponyewa mu Hadesi. Chifukwa ngati nchito zikulu zamane zachitiwa muli iwe asembe zinachitikiwa muli Sodoma, asembe nalelo ikaliko nalelo.
\v 24 Koma nikuuzani imwe kuti chizainkalilapo bwino ziko ya Sodoma pa siku ya chiweluzo kuchilapo imwe."
\s5
\v 25 Pa ntawi ija Yesu anakamba kuti, "Nikutamandani imwe, Atate, Ambuye wakumwamba na wa paziko lapansi, chifukwa munabisa ivi vintu kuli baja bantu banzelu na baja bomvesesa, koma mwavizibisa kuli bana bagóno.
\v 26 Zoona, Atate, chifukwa ichi chinali chinakumvesani bwino imwe.
\v 27 Vonse vintu vinapasiwa kuli ine kuchokela kuli ba Tate; futi kulibe wamene aziba Mwana koma chabe ba Tate, kulibe wamene aziba ba Tate koma chabe Mwana na muntu aliwonse wamene Mwana asanka kuti amuzibise.
\s5
\v 28 Bwelani kuli ine, bonse bamene mu sebenza mwalemesewa na katundu, ndipo nizakupasani kupumula.
\v 29 Tengani goli yanga pali imwe ndipo punzilani kuli ine, chifukwa ine ndine ozichepesa nafuti ozibwesa mutima, ndipo muzapeza kupula kwa moyo zanu.
\v 30 Chifukwa goli yanga siyovuta na katundu wanga niwopepuka."
\s5
\c 12
\cl Mutu 12
\p
\v 1 Pa ntawi ija Yesu anali ku enda-enda mu munda wa tiligu pa siku ya Sabata. Bopunzila bake banamvela njala bana yamba ku tyola tiligu naku dya.
\v 2 Koma pamene ba Falisi banaona ichi, banauza Yesu kuti, "Ona, bopunzila bako bachita chintu chamene chipwanya lamulo ya pa Sabata."
\s5
\v 3 Koma Yesu anabauza kuti, "Nanga munabelenga vamene Davide anachita pamene anamvela njala, pamozi na bamuna bamene anali nabo?
\v 4 Anaenda mu nyumba ya Mulungu nakudya buledi ya kupezekapo, chintu chamene sichinali chovomelesewa kuti adye na baja bamene banali pamozi na eve, koma chovomelesewa chabe kuli ba nsembe.
\s5
\v 5 Nanga simunabelenge mu malamulo kuti pa Sabata ba nsembe mu nyumba ya Mulungu bama pwanya Sabata koma balibe chimo?
\v 6 Koma niku uzani imwe kuti umozi mukulu ochila tempele alipo pamalo pano.
\s5
\v 7 Asembe munaziba chamene ichi chitantauza, 'Ine nifuna chifundo osati nsembe,' asembe simuna weluze muntu alibe chimo.
\v 8 Chifukwa Mwana wa Muntu ni Mfumu ya Sabata."
\s5
\v 9 Pamene apo Yesu anachokapo naku yenda mu Sinagogo yabo.
\v 10 Onani, munali muntu wamene anali na kwanja yoyuma. Ba Falisi banamufunsa Yesu, kuti, "Nanga nichovomelesewa kupolesa bantu pa Sabata?" kuti bamunamizile kuti achimwa.
\s5
\v 11 Yesu anakamba kuli beve kuti, "Nanga ni muntu uti pakati panu, wamene, ngati anali na nkosa imozi chabe, yamene iyi nkosa yabwela yagwela mu mugodi ukulu pa Sabata, sazai gwila nakuichosamo?
\v 12 Nanga nikuchilapo kwa bwanji, kansi, umoyo wa muntu pa wa nkosa! Chifukwa chake nichovomelesewa kuchita chintu chabwino pa Sabata."
\s5
\v 13 Pamene apo Yesu anakamba kuli uja mwamuna kuti, "Tembenula kwanja yako." Anaitembenula kwanja, inabwezewa kunkala ya tanzi, monga ija kwanja inangu.
\v 14 Koma ba Falisi bana enda naku yamba ku lingilila malingo pa umoyo wake. Banali kusakila njila yamene wanga mupaile.
\s5
\v 15 Pamene Yesu anaziba ivi, anachokako kumalo kuja. Bantu bambili banamukonka, ndipo anabachilisa bonse.
\v 16 Anabauza kuti basazibise bantu bali bonse pali eve,
\v 17 kuti chinkale cha zoona, chamene chinakambiwa kupitila muli muneneli Yesaya, kukamba kuti,
\s5
\v 18 "Onani, wantchito wanga wamene ninasanka; okondewa wanga, wamene moyo wanga umvela bwino. Nizaika Muzimu wnga pali eve, azalalikila chiweluzo kuli bakunja.
\s5
\v 19 Eve sazavutana kapena kupunda; kulibe wamene azamvela liu yake munjila.
\v 20 Sazatyola ntete yo onongeka; saza zimya nyali yamene ichosa chusi, kufikila pamene eve azasogolela kupambana,
\v 21 na muzina yake ba Kunja bazapezamo chiyembekezo."
\s5
\v 22 Umozi mpofu wamene anali chi ulu nafuti, wamene anali na chibanda, banamuleta kuli Yesu. Anamupolesa, kulengesa kuti uja muntu ayambe kuona naku kamba.
\v 23 Magulu yonse yanadabwa nakukamba kuti, "Nanga uyu mwamuna kansi angankale ndiye Mwana wa Davide?"
\s5
\v 24 Koma ba Falisi pamene banamvela va vodabwisa ivi, banakamba kuti, "Uyu muntu samachosa chabe vibanda asebenzesa Biluzibabu, mukulu wa vibanda."
\v 25 Koma Yesu anaziba maganizo yabo naku bauza kuti, "Ufumu uli onse wamene ugabika paweka uonongeka, na muzinda uli onse kapena nyumba yamene igabikana payeka siizaimilila.
\s5
\v 26 Ngata Satana achosa Satana, agabikana eka kansi. Nanga ufumu wake uzaimilila bwanji?
\v 27 Ngati ine nichosa vibanda kusebenzesa Belizababu, nanga bana banu basebenzesa chani? Chifukwa cha ichi nkalani boziweluzani mweka.
\s5
\v 28 Koma ngati ine nichosa vibanda kusebenzesa Muzimu wa Mulungu, ufumu wa Mulungu wabwela kuli imwe.
\v 29 Nanga muntu angangene bwanji mu nyumba ya muntu wampavu nakumubela vintu osayambilila kumangilila muntu wampavu? Akachita ichi anga kwanise nakuba vintu vake va munyumba.
\v 30 Uja wamene sali naine ashushana naine, nauja wamene sakololela pamozi naine ndiye wamene ataya.
\s5
\v 31 Chifukwa chake nikuuzani kuti, chimo ili yonse naku nyozela kuli konse muzakululukiliwa, koma kunyozela Muzimu sikuzakululukiliwa.
\v 32 Ali onse wamene akamba mau yonyoza Mwana wa Muntu, azakululikiliwa. Koma uja wamene anyozela Muzimu Oyela, uja sazakululukiliwa, muziko ino, kapena muziko yamene izabwela.
\s5
\v 33 Lengani mutengo unkale wabwino na vipaso vake vizankala vabwino, chifukwa mutengo umazibika na vipaso vake.
\v 34 Imwe bana banjoka, chifukwa ndimwe boipa, nanga mungakambe bwanji vintu vabwino? Chifukwa kuchokela mu kuzula kwa vintu vamene vili mu mutima ndiye vamene kamwa kakamba.
\v 35 Uja muntu wabwino kuchokela mu tumba yake yaku mutima yabwino amachosa vintu vabwino, na uja muntu oipa kuchokela mu tumba yake yaku mutima yoipa achosa voipa.
\s5
\v 36 Niku uzani kuti pa siku yoweluza bantu bazakaweluziwa pa mau yali yonse yamene yalibe pindu yamene bakamba.
\v 37 Chifukwa ni mu mau yako mwamene iwe uzaonesa kulangama, na mu mau ndiye mwamene uzaweluziliwa."
\s5
\v 38 Pamene apo bena bolemba na ba Falisi banamuyanka Yesu kuti, "Mupunzisi, ise tifuna kuona choonesa kuli iwe."
\v 39 Koma Yesu anabayanka kuti, "Mubadwe oipa wachigololo ufuna cho-onesela. Koma kulibe cho-onesela chamene chizapasiwa koma chabe cho-onesela cha Yona muneneli.
\v 40 Monga mwamene Yona analili ma siku yatatu na mazuba yatatu mu mala mwa chinsomba chikulu, chimozo-mozi mwamene Mwana wa Muntu azankalila masiku yatatu na mazuba yatatu mu mutima wa ziko.
\s5
\v 41 Bantu baku Nineve bazakaimilila pa siku yoweluza pamozi na mubadwe uyu naku iweluza. Chifukwa beve banatembenuka chifukwa cha kulalikila kwa Yona, koma onani, mukulu ochila na pali Yona ali po pano.
\s5
\v 42 Mfumu mukazi wakumwela azakaimilila pa siku yoweluza pamozi na bantu ba mubadwe uno naku baweluza. Eve anabwela kuchokela kosilizila ziko kuti akamvele nzelu za Solomoni, koma onani, muntu mukulu pali Solomoni ali pano.
\s5
\v 43 Pamene muzimu wadoti uchoka mumuntu, uma pita mu malo yamene yalibe manzi kusakila popumulila, koma siu upeza.
\v 44 Pamene apo ukamba kuti, 'Nizabwelela ku nyumba yanga kwamene ine ninachokela.' Pamene ubwelela, upeza kuti nyumba ija niyopyangiwa na vintu voikiwa mumalo mwake.
\v 45 Umabwela waenda kukatenga kubwela nazo mizimu zinangu zili seveni zamene zinkala zoipisisa kuchila yeve, babwela naku nkala mukati mwake muntu uyu. Posilizila pake nipakuti uja muntu azankala ochilapo kulinganisana na poyamba. Nimwa mene chizankalila na uyu mubadwe oipa."
\s5
\v 46 Pamene Yesu anali akali kukamba na gulu ya bantu, onani, ba mai bake na babale bake banaimilila panja, kufuna kuti bakambe na eve.
\v 47 Umozi pali eve anakamba kuli eve kuti, "Onani, bamai bako na babale bako bali imilile panja, bafuna kukamba naiwe."
\s5
\v 48 Koma Yesu anayanka nakukamba kuli eve kuti, "Nanga nindani mai wanga kapena nibati ba bale banga?"
\v 49 Pamene apo anatambasula kwanja yake kulangiza kunali bopunzila bake nakukamba kuti, "Onani, aba bali apa ba mai banga na babale banga!
\v 50 Chifukwa muntu ali onse wamene achita chifunilo cha ba Tate banga bamene bali kumwamba, uja muntu ndiye mubale wanga, mulongo wanga, mai wanga."
\s5
\c 13
\cl Mutu 13
\p
\v 1 Pa siku yamene ija Yesu ana enda panja pa nyumba naku nkala pambali pa nyanja.
\v 2 Gulu ikulu ina unjikana kumuzungulukila, pamene apo anangena mu bwato naku nkala mwamene muja pamene gulu yonse inaimilila posilizila nyanja.
\s5
\v 3 Yesu anakamba nabo vintu vambili kupitila mu myambo. Anakamba kuti, "Onani, mulimi anaenda kuka shanga mbeu.
\v 4 Pamene anali kushanga, mbeu zinangu zinagwela mumbali mwa museu, tunyoni tunabwela twaizidya.
\v 5 Zinangu mbeu zinagwela pa myala, pamene zinalibe ntaka yambili. Pamene apo zinamela chifukwa ntaka siinali yongena pansi maningi.
\v 6 Koma pamene zuba inaima, zina ochewa chifukwa zinalibe mizyu, ndipo zinayuma.
\s5
\v 7 Mbeu zinangu zinagwela pakati pa minga. Minga zinamela naku kama mbeu izi.
\v 8 Zinangu mbeu zinagwela pa ntaka yabwino zinamela naku nkala na vipaso vabwino, zinangu makumi yali kumi kuchilapo, zinangu makumi asanu na imozi, ndipo na yenangu makumi yatatu.
\v 9 Wamene ali na matu, mulekeni amvele."
\s5
\v 10 Bopunzila banabwela kuli Yesu nakukamba kuti, "Nanga nichani mukamba nagulu mu myambo?"
\v 11 Yesu anaba yanka kuti, "Imw munali nao mwai womvesesa vobisika va mu ufumu waku mwamba, koma kuli beve sichina pasiwe ichi.
\v 12 Chifukwa kuli wamene ali navo vambili vizapasiwa, ndipo azankala navambili. Koma kuli uja wamene alibe, na vamene ali navo vizapokewa.
\s5
\v 13 Ichi ndiye chifukwa chake chamene nibauzila kupitila mu miyambo: ngakale kuti babelenga, koma sibaona; bangankale bamvela, koma sibamvesesa.
\v 14 Kuli beve uneneli wa Yesaya ufikilisiwa, wamene unakamba kuti, 'Ngakale kuti kumvela muzayamba kumvela, koma kulibe njila yamene muzamveseselamo; ngakale kuti muona, koma kulibe njila yamene munaonelamo.
\s5
\v 15 Chifukwa mitima za aba bantu zinankala zosamvela, sibamvela naku mvela, ndipo bana vala na menso yabo, kuti basakwanise kuona na menso yabo, kapena kumvel na matu yabo, kapena kumvesesesa na mitima zabo, kuti batem enuke, kuti ine niba polese.'
\s5
\v 16 Koma menso yanu niyodalisika, chifukwa yaona; na matu yanu, chifukwa ya mvela.
\v 17 Zoona nikuuzani imwe kuti bambili baneneli na bantu bolungama banali kufunisisa kuti baone vintu vamene imwe muona koma sibana vione. Banafunisisa kuti bamvele vintu vamene imwe mumvela kuma sibana vimvele.
\s5
\v 18 Mvesesani kuli ntano ya mulimi wamene ana shanga mbeu zake.
\v 19 Pamene muntu ali onse amvela mau ya ufumu koma samvesesa tantauzo yake, uja oipa amabwela naku jompola chamene chashangiwa mumutima wake. Iyindiye mbeu yamene inali inashangiwa mumbali mwa museu.
\s5
\v 20 Chamene chinashangiwa pa myala ni uja muntu wamene amamvela mau na pamene apo amayalandila mokondwela,
\v 21 koma alibe mizyu muli eve ama limbikila pangóno chabe. Pamene mavuto kapena kuvutikisiwa kubwela chifukwa cha mau, akugwa kamusanga.
\s5
\v 22 Chamene chinashangiwa pakati pa minga, ndiye uja muntu wamene amamvela mau, koma kukonda va muziko na boza ya chuma vima kama mau aya, ndipo ankala alibe vipaso.
\v 23 Mbeu yamene imashangiwa pa ntaka ya bwino, niuja muntu wamene amamvela mau naku yamvesesa. Ama nkala na vipaso, kubala mumozi handeledi, mwinangu sikiste, na mwinangu ma sate kupitililapo pali vamene anashanga."
\s5
\v 24 Yesu anabapasa myambo ina. Anakamba kuti, "Ufumu wa kumwamba uli monga muntu wamene anashanga mbeu yabwino mu munda wake.
\v 25 Koma pamene anali gone, mudani wake anabwela naku shanga mau uzu pakati pa tiligu naku yenda.
\v 26 Pamene matepo yanamela naku nkala na vipaso vabo, na mauzu yanaonekela na yeve.
\s5
\v 27 Ba ntchito ba uja mwine wa munda anabwela nakukamba kuli eve kuti, 'Bwana, nanga kansi siti nashange mbeu yabino yeka chabe? Nanga nichani mwamela mau uzu?'
\v 28 Anaba yanka kuti, 'Mudani ndiye wamene achita ivi.' "Bantchito bana kamba kuti, 'Nanga mungativomeleze kuti tiyende tikayanyule mau uzu?'
\s5
\v 29 "Mwine wa munda anayanka kuti, 'Iyayi. Chifukwa pamene imwe muzayamba kunyula mau uzu, munganyulile pamozi na tiligu.
\v 30 Vilekeni vimelele pamozi chabe. Pa ntawi yokolola nizakabauza bokolola kuti, "Yambililani kuchosa ma uzu muyamangilile nakuyamangilila muya oche naku yaocha, koma tiligu yeve muyi kolole mui ike mu chibaya changa.'""
\s5
\v 31 Yesu anabauza mwambo winangu beve. Anakamba kuti, "Ufumu waku mwamba uli monga ka mbeu kampiru kamene muntu anatenga naku shanga mu munda wake.
\v 32 Aka kambeu nika ngóno pa mbeu zonse. Koma kaka kula, ndiye kankala kakulu pali vomela vonse mumunda. Chimankala chimutengo, mwakuti tu nyoni twa kumwamba tumabwela naku pumulila muli cheve."
\s5
\v 33 Yesu pamene apa anabauza mwambo wina. "Ufumu waku mwamba uli monga chotupisa chamene muzimai anatenga naku ika mu vigawa vitatu va fulawa kufikila mpaka fulawa ija inatukumuka."
\s5
\v 34 Vonse ivi vintu Yesu anali ku uza magulu kupitila mu myambo; sanali kukamba na babo bantu bantu ngati sanasebenzese myambo.
\v 35 Chifukwa chake chinali chakuti vintu vamene vina kambiwa na muneneli vikachitike, pamene anakamba kuti, "Niza segula kamwa kanga mu myambo. Niakamba vintu vamene vinali vobisika kuchokela koyambila kwa ziko."
\s5
\v 36 Pamene apo Yesu anayasiya magulu naku enda munyumba. Bopunzila bake banabwela kuli eve nakukamba kuti, "Tiuzeni tantauzo ya myambo ya ma uzu mu munda."
\v 37 Yesu anabayanka nakukamba kuti, "Uja wamene ashanga mbeu ni Mwana wa Muntu.
\v 38 Munda ni ziko; ija mbeu yabwino, ndiye baja bana bamu ufumu. Mau uzu ndiye bana ba mudani,
\v 39 mudani wamene anashanga mbeu zija ni mudani. Kukolola ndiye kusila kwa mubadwe, bokolola ni bangelo.
\s5
\v 40 Chifukwa chake, monga mwamene mauzu bamaya chosela naku yashoka na mulilo, ndiye mwamene chizankalila paku sila kwa mubadwe.
\v 41 Mwana wa Muntu azaka tuma bangeli bake, bazaka ika pamozi kuchosa mu ufumu wake vintu vonse vamene vima lengesa kuchimwa nabaja bamene bachita machimo.
\v 42 Bazaba taya mumuli, mwamene muzankala kulila naku sheta meno.
\v 43 Pamene apo baja bolungama bazaka unikila monga zuba mu ufumu waba Tate wabo. Wamene ali na matu, mulekeni amvele.
\s5
\v 44 "Ufumu wa kumwamba uli monga chuma chamene chinavisiwa mu munda. Muntu anachipeza nakuchibisa. Mukukondwela kwake aenda, nakugulisa vintu vake vonse vamene alinavo, naku gula uja munda.
\v 45 Chimozi-mozi, ufumu wa kumwamba uli monga muntu wamalonda wamene asakila sakila myala zamutengo wapatali.
\v 46 Pamene anapeza mwala umozi wamutengo wapatali, anaenda naku gulia vonse vamene anali navo naku ugula.
\s5
\v 47 "Futi, ufumu waku mwamba uli monga chokokela nsomba chamene chinaponyewa mu nyanja, chamene china gwila vintu vosiya siyana.
\v 48 Pamene china zula, bogwila nsomba banachi donsa kuchileta kumbali kwa manzi. Bana nkala pansi naku tengamo vija vabwino kuvi ika muma lubango, koma vija vamene vinalibe ntchito banavitaya.
\s5
\v 49 Chizakankala chimozi-mozi pa kusila kwa mubadwe. Bangeli bazakabwela naku patulisa baja boipa kobachosa kuli baja bolungama.
\v 50 Bazabataya mumulilo, mwamene muzankala kulila naku sheta meno.
\s5
\v 51 "Nanga mwamvesesa ivi vintu mwati?" Bopunzila bake banamuyanka naku kamba kuti, "Eeeh."
\v 52 Pamene apo Yesu anabauza kuti, "Chifukwa cha ichi ali onse kalembela wamene ankala opunzila mu ufumu waku mwamba ali monga muntu wamene ndiye mwine wa nyumba, wamene achosa vintu vonse vasopano navija vakudala kuchosa mosungila mwake."
\v 53 Pamene Yesu anasiliza izi myambo, anachokako kuja kumalo.
\s5
\v 54 Yesu anabwelela kumalo kwake naku yamba kupunzisa bantu muma Sinagogo yabo. Pindu yake inali yakuti banali bodabwa kwambili naku kamba kuti, "Kansi uyu muntu izi nzelu azichosa kuti na ivi vodabwisa?
\v 55 Nanga uyu siwamene mwana wa mupala ma tabwa? Nanga mai wake siuja Maria? Nanga wabale bake sibaja bene Yakobo, Yosefe, Simoni, na Yudasi?
\v 56 Nanga balongo bake sitinkala nabo kansi? Nanga ivi vintu vonse kansi anavichosa kuti?"
\s5
\v 57 Banakalipa naye. Koma Yesu anabauza kuti, "Muneneli amalandila ulemu kuli konse kuchoselako chabe mu ziko yake na ku banja yake."
\v 58 Sanachite vodabwisa vambili kuja chifukwa cha kukana kukulupilila kwabo.
\s5
\c 14
\cl Mutu 14
\p
\v 1 Pantawi ija, Helodi umozi mwa basogoleli anamvela uthenga wa Yesu.
\v 2 Anauza bantchito bake kuti, "Uyu niwamene Yogane Obatiza; auka kubakufa. Ndiye chamene chilengesa mpavu kusebenza muli eve."
\s5
\v 3 Chifukwa Helodi anamugwila Yohane, nakumumanga, nakumuika mu ndende chifukwa cha Helodiyasi, mukazi wa Filipu mubale wake. Chifukwa
\v 4 Yohane anamuuza kuti, "Sichintu chovomelesewa kuti uyu ankale mukazi wako."
\v 5 Helodi anafuna kumupaya, koma anali kuyopa bantu, chifukwa banali kumuyopa kukamba kuti nimuneneli.
\s5
\v 6 Koma siku yokumbukila kubadwa kwa Helodi inafika, mwana mukazi wa Helodiyasi anavina pakati pa bantu nakumvesa bwino Helodi.
\v 7 Pakuona ichi, anamulonjeza lonjezo molapa kuti azamupasa chintu chili chonse chamene azapempa.
\s5
\v 8 Pamene bamai bake banamuuza vopempa, anakamba kuti, "Nipaseni apa manje, pa mbale, mutu mwa Yohani Obatiza."
\v 9 Mfumu inakalipa maningi chifukwa cha chamene anapempa, manje chifukwa chakuti analapa na chifukwa cha baja bantu bamene banali naye pa chakudya chaku mazulo, anakamba kuti ichi chamene chichitike.
\s5
\v 10 Anatumiza kuti bayende bamupaye Yohane mu ndende.
\v 11 Ndipo mutu wake unabwelesewa pa mbale naku pasiwa kuli mwana mukazi uja wamene anautenga naku upeleka kuli bamai bake.
\v 12 Bopunzila bake banabwela, nakunyamula thupi yake, naku yenda kuiika mumanda. Kuchoka apa, banayenda kukamuuza Yesu.
\s5
\v 13 Manje pamene Yesu anamvela ichi, anachokako uku naku enda ku malo kwa eka. Pamene magulu yanamvela ichi, banamukonnka Yesu na mendo kuchokela mu mizinda.
\v 14 Yesu anabwela kwamene kunali beve nakuona gulu ikulu maningi. Anamvela chifundo nakubapolesela bantu bodwala babo.
\s5
\v 15 Ntawi yaku mazulo, bopunzila banabwela kuli eve nakumuuza kuti, "Kuno kumalo kulibe bantu, na ntawi yasila. Balekeni bantu, basiyeni bayende mu minzi kuti bakagule vakudya badye."
\s5
\v 16 Koma Yesu anabayanka kuti, "Aba sibafunika kuti baende iyayi. Imwe mubapase vakudya."
\v 17 Koma banamuyanka kuti, "Onani tili chabe na buledi ili 5 na nsomba zibili."
\v 18 Yesu anayanka kuti, "Letani kuli ine."
\s5
\v 19 Yesu anauza gulu kuti inkale pansi pa mauzu. Anatenga ma buledi yaja na nsomba zibili. Analangana kumwamba, anayadalisa ma buledi nakuya suna naku pasa bopinzila bake, na bopunzila bake banapasa ija gulu ya bantu.
\v 20 Bonse banadya naku kuta. Banatenga vamene vinasalapo - votengelamo vili kumi na vibili.
\v 21 Baja bamene banadya banali 5000 bamuna, kochoselako bakazi na bana.
\s5
\v 22 Pamene apo anauza bopunzila bake kuti bangene mu bwato bayende kumbali kwina kwa nyanja, pamene eve anali kupisha bantu.
\v 23 Pamene anasiliza kupisha bantu, anayenda pa chulu eka nakupempela. Pamene usiku unabwela, analipo eve eka.
\v 24 Koma bwato inali kutali pakati pa manzi, inali kugwedezeka na chimpepo, chifukwa chimpepo chinali chikulu.
\s5
\v 25 Mbanda kucha Yesu anafika kufupi na beve, nishi ayenda pa manzi.
\v 26 Pamene bopunzila bake banamuona ayenda pa manzi, banavutika mutima nakukamba kuti, "Nichibanda," banalila na manta.
\v 27 Koma Yesu anabauza pamene apo kuti, "Nkalani bolimba! Ndine! Osayopa iyayi."
\s5
\v 28 Petulo anamuyanka nakukamba kuti, "Ambuye, ngati ndimwe, niuzeni kuti ine nibwele pa manzi."
\v 29 Yesu anakamba kuti, "Bwela." Pamene apo Petulo anachoka mu bwato naku yenda pa manzi kuyenda kuli Yesu.
\v 30 Koma pamene Petulo anaona chimpepo, anayopa, pamene anayamba kumbila, analila nakukamba kuti, "Ambuye, nipulumuseni!
\s5
\v 31 Yesu pamene apo anatambasula kwanja yake, nakumugwila Petulo, nakumuuza kuti, "Iwe wachikululupilo chingóno, nanga nichani chamene wenze wakaikilila?"
\v 32 Manje pamene Yesu na Petulo banangena mu bwato, chimpepo chija chinaleka.
\v 33 Baja bopunzila bake bamane banali mu bwato banamupembeza Yesu naku kamba kuti, "Zoona ndimwe Mwana wa Mulungu."
\s5
\v 34 Pamene beve banafika kumbali kwinangu kwa nyanja ija, banafikila kumalo yaku Genezaleti.
\v 35 Pamene bantu bakuja kumalo banamuziba Yesu, bana tuma mau monse mu malo ya mumbali, ndipo banaleta bantu bonse bodwala.
\v 36 Banamupapatila kuti bagwileko chabe chovala chake, ndipo bonse bamene banamugwila banapolesewa.
\s5
\c 15
\cl Mutu 15
\p
\v 1 Ba Falisi naba Bolemba banabwela kuli Yesu kuchokela ku Yelusalemu. Banakamba kuti,
\v 2 "Nanga nichani bopunzila bako sibakonka myambo za makolo? Chifukwa sibasamba kumanja pakudya."
\v 3 Anabayanka kuti, "Nanga naimwe nichani chamene mupwanyila lamulo ya Mulungu chifukwa cha myambo zanu?
\s5
\v 4 Chifukwa Mulungu anakamba kuti, 'Lemekeza batate bako na bamai bak', nafuti kuti 'Eve wamene anyoza ba tate bake kapena bamai bake azapaiwa.'
\v 5 Koma imwe mukamba kuti, 'Ali onse wamene auza tate wake kapena mai wake kuti, "Tandizo ili yonse yamene imwe munalandila kochokela kuli ine ni mpaso yopelekewa kuli Mulungu,"
\v 6 wamene uja muntu futi safunikila kulemekeza batate bake.' Chifukwa cha ichi mwalengesa kuti mau ya Mulungu yankala yalibe mpavu chifukwa cha myambo zanu.
\s5
\v 7 Imwe bantu baboza! Zoona mwamene Yesaya ananenela pali imwe pamene anakamba kuti,
\v 8 'Aba bantu banilemekeza chabe pakamwa, koma mitima zabo zili kutali na ine.
\v 9 Bapembeza ine mwachabe chifukwa bapunzisa kunkala vipunziso malamulo ya bantu.'"
\s5
\v 10 Anabwela aitana gulu kuti ibwele kuli eve naku iuza kuti, "Mvelani nafuti mumvesese-
\v 11 Kulibe chintu chamene chingena mukamwa naku lakwisa muntu uyo. Koma, chamene chichoka mukamwa, ndiye chamene chima lakwisa muntu.
\s5
\v 12 Bopunzila banabwela naku mu-uza Yesu kuti, "Nanga muziba kuti ba Falisi bamakalipa bakamvela mau aya?"
\v 13 Yesu anabayanka nakukamba kuti, "Mutengo uli onse wamene ba Tate banga sibana shange uzanyuliwa.
\v 14 Basiyeni beka, nibasogoleli balibe menso. Ngati mpofu asogolela mpofu winangu, bonse bazagwela mumugodi."
\s5
\v 15 Yesu anayanka nakukamba kuti, "Tiuzeni chikambidwe ichi."
\v 16 Yesu anayanka kuti, "Naimwe monse simuziba kukamba uku?
\v 17 Nanga simumaona kuti chintu chilichonse chamene chingena mukamwa chima enda mumala naku choka kuyenda muchimbuzi?
\s5
\v 18 Koma vintu vamene vamachoka mukamwa vimachokela mumutima. Ivi ndiye vintu vamene viononga muntu.
\v 19 Chifukwa mumutima wa muntu ndiye mwamene mumachokela maganizo yoipa, kupaya, vigololo, uchiwelewele, ukawalala, ukamboni waboza, na kunyozela.
\v 20 Ivi ndiye vintu vamene vima ononga muntu. Koma kudya pamene sunasambe kumanja sikumaononga muntu.
\s5
\v 21 Pamene apo Yesu anenda kuchoka kuja kumalo naku yenda kumalo yaku dela yaku Taya naku Sidoni.
\v 22 Onani, muzimai waku Kanani anabwela kuchoekela kumalo yaja. Anapunda naku kamba kuti, "Nimvelelenikoni chifundo ine, Ambuye, Mwana wa Davide! Mwana wanga mukazi atengewa maningi nachibanda."
\v 23 Koma Yesu sanamuyanke mau yali yonse muzimai uyu. Bopunzila bake banabwela nakumupapatila kukamba kuti, "Mupisheni uyu aende, chifukwa atipundila ise."
\s5
\v 24 Koma Yesu anayanka naku kamba kuti, "Ine sininatumiwe ku muntu ali onse koma chabe kuli nkosa za munyumba ya Izilayeli."
\v 25 Koma anabwela naku gwada pamenso pake, nakukamba kuti, Ämbuye, nitandizeni ine."
\v 26 Anamuyanka naku kamba kuti, "Sichintu chabwino kutenga buledi yabana naku itaila kuli tu imbwa tubana."
\s5
\v 27 Anakamba kuti, "Zo-ona, Ambuye, koma na tu imbwa tungóno tumadya votaikila kuchoka podyela bene bake."
\v 28 Pamene apo Yesu anayanka nakumuuza eve kuti, "Muzimai, uli na chikulupililo chikulu; leka chikuchitikile monga mwamene iwe ufunila." Pamene apo mwana wake mukazi uja anapola.
\s5
\v 29 Yesu anachokako kumalo kuja naku yenda ku nyanja yaku Galileya. Anaenda akwela pa lupili naku nkala pamene paja.
\v 30 Magulu yabantu yanamukonka. Banamuletela bantu bolemala, mpofu, bachi ulu, na bantu bopunduka, na baja bamene banali bodwala. Banabaika pafupi na Yesu, anabapolesa.
\v 31 Gulu ija inadabwa kwambili pamene banaona bachi ulu bayamba kukamba, bopunduka bapola, bolemala bayenda, na mpofu ziona. Banatamanda Mulungu waku Izilayeli.
\s5
\v 32 Yesu anaitana bopunzila bake nakubauza kuti, "ine gulu ya bantu yanimvesa chifundo chifukwa chakuti bankala naine masiku yatatu pamene apa koma balibe na vakudya. Sinifuna kuba pisha bakalibe kudya kali konse, chifukwa banga komoke munjila."
\v 33 Bopunzila banamuuza kuti, "Manje nanga nikuti kwamene tingagule mukate wamene ungakwanile kudyesa gulu ikulu iyi ya bantu kuno kumalo kwamene sikunkala na bantu?"
\v 34 Yesu anabayanka kuti, "Nanga ma buledi yamene muli nayo niya ngati? Bana yanka kuti, "Yali seveni, na tu nsomba tungóno."
\v 35 Yesu anabauza gulu ija kuti inkale pansi."
\s5
\v 36 Anatenga ma buledi yali seven yaja na nsomba, pamene ana yamika, ana suna ma buledi yaja naku yapasa kuli bopunzila bake. Bopunzila bake bana gabisa gulu.
\v 37 Bantu bonse banadya naku kuta. Bana tenga ma buledi yanasalako muma basketi.
\v 38 Baja bamene banadya banali four sauzande bamuna, kosapendelako bazikazi na bana.
\v 39 Kuchoka apa Yesu anapisha yaja magulu kuti yayende pamene apo anakwela mu bwao naku yenda ku malo yaku Magadana.
\s5
\c 16
\cl Mutu 16
\p
\v 1 Ba Falisi naba Saduki banabwela kumuyesa eve kumufunsa kuti abalangise cholangiza chokokela kumwamba.
\v 2 Koma anabayanka nakubauza kuti, "Pamene ikali ntawi yaku mazulo, mumakamba kuti, 'Kuzankala bwino lelo, chifukwa makumbi yaoneka monga ma magazi.'
\s5
\v 3 Pamene kukucha, mumakamba kuti, 'lelo kzankala mpepo, chifukwa makumbi yaoneka monga magazi nafuti yavala kumwamba.'Imwe muziba tantauzo ya kaonekedwe ka makumbi, koma mukangiwa kuziba voonesa ntawi.
\v 4 Mubadwe woipa wa chigololo ifunisisa choonesa, koma kulibe choonesa chamene chizapasiwa koma cha Yonah cheka." Pamene apo Yesu anabasiya naku enda.
\s5
\v 5 Pamene bopunzila banafika kumbali ina, banaibala kunyamula buledi.
\v 6 Yesu anabauza kuti, "Nkalani bochenjela ku votupisa vaba Falisi na ba Saduki."
\v 7 Bopunzila banayamba kukambisana pakati pabo kuti, "Nichifukwa chakuti sitinanyamule buledi."
\v 8 Yesu anaziba kuganiza kwabo nakubauza kuti, "Imwe ba chikulupililo chingóno, nanga nichani mukambisana pamweka kuti nichifukwa chakuti simunanyamule buledi?
\s5
\v 9 Nishi simuona kapena kukumbuka ma buledi yaja yanali 5 ya bantu banali 5000, na mabasiketi yamene munatengelamo vinasala?
\v 10 Kapena ma buledi yanali 7 ya bantu banali 4000, na mabasiketi yamene yanasalapo yamene munatenga?
\s5
\v 11 Nanga nibwanji imwee simuona kuti sininali kukamba naimwe pali buledi? Nkalani wochenjela na votupisa vaba Falisi naba Saduki."
\v 12 Pamene apa banaziba kuti sanali kubauza kuti basachenjele chifukwa cha chotupisa cha buledi, koma kuti bankale wochenjela chifukwa cha vipunziso vaba Falisi naba Saduki.
\s5
\v 13 Pamene Yesu anabwela kumalo pafupi na Sizaliya na Filipi, anabafunsa bopunzila bake kuti, "Nanga bantu kansi bakamba kuti Mwana wa Muntu nindani?"
\v 14 Banamuyanka kuti, "Benangu bakamba kuti ndiwe Yohane Mubatizi; benangu bakamba kuti Eliya; na benangu, Yelemiya, kapena umozi opunzila wa baneneli."
\v 15 Anabauza kuti, "Nanga imwe mukamba ine ndine ndani?"
\v 16 Mukuyanka, Simoni Petulo anakamba kuti, "Ndimwe Kristu, Mwana wa Mulungu wa moyo."
\s5
\v 17 Yesu anayanka naku muuza kuti, "Ndiwe odalisika, Simoni mwana wa Yonah, chifukwa tupi na magazi sivamene vakuzibisa ichi, koma ba Tate banga bamene bali kumwamba.
\v 18 Nikuuza futi kuti iwe ndiwe Petulo, pa mwala wamene uyu ine nizamanga kachisi yanga. Viseko vaku Hadesi sivizakwanisa kupambana.
\s5
\v 19 Nizakupasa mfungulo yaku ufumu wa kumwamba. Chilichonse chamene uzamanga pa ziko ya pansi chizamangiwa kuziko yaku mwamba, na chili chonse chamene uzamangusula paziko yapansi chimangusuliwa kumwamba."
\v 20 Yesu anauza bopunzila bake kuti basauzeko muntu aliwonse kuti eve ni Kristu.
\s5
\v 21 Kochokela ntawi yamene iyo Yesu anayamba kuuza wopunzila bake kuti eve afunika kuyenda ku Yelusalemu, akavutikisiwe mu vintu vambili mumanja yaba kulubakulu na bakulu ba nsembe na bolemba, akapaiwe, koma akauke kubakufa pa siku ya chitatu.
\v 22 Petulo anamutenga kumbali Yesu naku mukalipila, kukamba kuti, "Ichi chinkale kutali naimwe, Ambuye; osati ivi vikakuchitikileni imwe."
\v 23 Koma Yesu anapindamuka nakuuza Petulo kuti, "Yenda kumbuyo kwanga ine, Satana! Ndiwe chogwesa ine, chifukwa susamalila vintu va Mulungu, koma chabe va bantu."
\s5
\v 24 Yesu anakamba kuli bopunzila bake kuti, "Ngati muntu aliwonse afuna kunikonka ine, ayenela kuzikana eka, anyamule mutanda wake, anikonke.
\v 25 Chifukwa aliwonse wamene afuna kupulumusa moyo wake azautaya, na uja wamene ataya moyo wake chifukwa cha ine azaupeza.
\v 26 Nanga pindu ilipati ngati muntu atenga ziko yonse koma ataya moyo wake? Nichichani chamene muntu angapase kuchinjanisa na moyo wake?
\s5
\v 27 Chifukwa Mwana wa Muntu azakabwela mu ulemelelo waba Tate bake pamozi nabangelo bake. Kuchoka apa azakapasa muntu aliwonse malipilo kulingana navamene anachita.
\v 28 Zoona nikuuzani imwe, pali benangu bamene bali imilile pano bamene sibazakaona imfa mpaka bakaone Mwana wa Muntu mu ufumu wake."
\s5
\c 17
\cl Mutu 17
\p
\v 1 Ma siku yokumana yali sikisi Yesu anatenga Petulo, Yakobo, na Yohane mubale wake, nakukwela nabo pamwamba pa lupili pa beka.
\v 2 Anachinjisiwa pamenso pabo. Pa menso pake pabala monga zuba, na vovala vake vinankala vobala monga nyali.
\s5
\v 3 Onani, banaonekela kuli beve Mose na Eliya ndishi bakamba na eve.
\v 4 Petulo anavula kamwa nakukamkba kuli Yesu kuti, "Ambuye, nichabwino kuti ise kupeza pano. Ngati mufuna, nizapanga pano tu mitenge tutatu-kamozi kani, kamozi ka Mose na kenangu ka Eliya."
\s5
\v 5 Pamene eve anali kukamba, onani, kumbi inaba vundikila, ndipo onani, munachoka mau mu kumbi, yokamba kuti, "Uyu ndiye Mwana wanga Wokondewa, wamene ine nimvela bwino. Mumveleleni."
\v 6 Pamene bopunzila banamvela ivi, banagwada pansi namanta.
\v 7 Yesu anabwela abagwila na kwanja nakukamba kuti, "Imani musachita manta."
\v 8 Pamene apo banalanga kumwamba koma sibanaone ali onse koma Yesu eka chabe.
\s5
\v 9 Pamene banali kubwelela kuchoka pa lupili, Yesu anabauza, kuti, "Musa uzeko muntu ai onse pali ivi vamene mwaona koma pamene Mwana wa Muntu azaka ukishiwa ku bakufa."
\v 10 Bopunzila bake banamufunsa, kuti, "Nanga nichani bolemba bama kamba kuti Eliya ndiye wamene ayenela kuyambilila kubwela?"
\s5
\v 11 Yesu anabayanka nakukamba kuti, "Eeeh Eliyah ndiye wamene azayambilila kubwela kukonza vintu vonse.
\v 12 Koma nikuuzani imwe kuti, Eliya anabwela kudala, koma sibanamuzibe. Koma, banamuchitila vonse vamene banali kufuna kuli eve. Chimozi-mozi, Mwana wa Muntu azakavutika mumanja yabo."
\v 13 Pamene apo bopunzila bake banaziba kuti anali kuba uza pali Yohane Obatiza.
\s5
\v 14 Pamene banabwela kumene kunali gulu yabantu, mwamuna umozi anabwela kuli eve, anagwada pansi, naku kamba kuti,
\v 15 "Ambuye, chitilanikoni chifundo mwana wanga, chifukwa adwala makate ndipo amavutika maningi. Kambili amagwela pa mulilo penangu mumanzi.
\v 16 Nenze namu leta kuli bopunzila banu, koma bakangiwa kumupolesa."
\s5
\v 17 Yesu anamuyanka, "Bosakulupilila mubadwe oónongeka, kansi ninkale naimwe ntawi itali bwanji? Kansi ninkale ozigwila ntawi itali bwanji? Muleteni kuno kuli ine."
\v 18 Yesu anachikalipila chija chi muzimu, chinachoka nochoka muli eve chija chimuzimu, na uja mwana anapola ntawi yamene ija.
\s5
\v 19 Bopunzila banabwela kuli Yesu pa beka nakukamba kuti, "Nanga nichani chamene ise takangiwila kuchichosa?"
\v 20 Yesu anayanka kuti, "Chifukwa ndimwe bochepa chikulupililo. Niku-uzani kuti, ngati muli nacho chikulupililo olo chochepa monga ka mbeu kampilu, munga chi uze ichi chi lupili kuti, 'Choka apa uyende paja,' ndipo chizafendela, kuli chamene chizankala choshupa kuli imwe." Ma buku yenangu yakudala maningi yalibe ndime ya 21
\v 21 "Koma ivi va mutundu uyu sivima choka koma ngati mwazimana chakudya na pempelo."
\s5
\v 22 Pamene bakanali mu muzinda wa Galileya, Yesu anauza bopunzila bake kuti, "Mwana wa Muntu aza pelekewa mumanja ya bantu,
\v 23 ndipo bazamupaya, koma pa siku ya chitatu azakaukishiwa kubakufa." Bopunzila bake banankala bokalipa.
\s5
\v 24 Pamene banafika mu muzinda wa Kapenamu, bantu baja bamene banali kutenga ndalama za mu tempele banabwela kuli Petrosi nakumuuza kuti, "Nanga bapunzisi banu bamalipila musonko wamu tempele?"
\v 25 Anabayanka kuti, "eeeh." Pamene Petrosi anabwela munyumba, Yesu anamufunsa kuti, "Nanga iwe uganizapo bwanji, Simoni? Nanga nikuli bandani kwamene mfumu za pa ziko zima tengako musonko kapena volipilisa? Kuli bana babo kapena bantu benangu chabe?"
\s5
\v 26 "Kuli bantu benangu chabe," Petulo anabayanka. Kansi ndishi bana nibomasuka," Yesu anamuyanka.
\v 27 Koma kuti ise tisa lengese bantu bamusonko kuti bachimwe, enda ku nyanje, uponye musozo, utenge nsomba yamene izayambilila gwiliwa. Uivule kamwa, uzapezamo ndalama. Itenge uyende ukapase bamusonko kulipilila iwe na ine."
\s5
\c 18
\cl Mutu 18
\p
\v 1 Pantawi yamene ija bopunzila ba Yesu banabwela kuli eve naku mufunsa kuti, "Nanga nindani mukulu mu ufumu wa kumwamba?"
\v 2 Yesu pamene apo anaitana ka mwana kangóno, naku kaika pakati pabo,
\v 3 nakukamba kuti, "Zoona ni kuuzani imwe, ngati chabe mwatembenuka naku nkala monga kamwana kangóno aka, simuzakangena mu ufumu waku mwamba.
\s5
\v 4 Chifukwa chake, ali onse wamene azichepesa kunkala monga ka mwana kangóno aka ndiye mukulu mu ufumu waku mwamba.
\v 5 Alionse wamene alandila kamwana kangóno monga aka muzina yanga alandila ine.
\v 6 Koma ali onse wamene alengesa mwana ali onse wamene akulupilila muli ine kuti achimwe, chawamapo kuti amangiwe kuchi mwala chikulu, naku muponya pansi pa manzi.
\s5
\v 7 "Soka kuli ziko chifukwa cha vintu vamene vigwesana! Chifukwa nichofunikila kuti vintu vogwesa vibwele, koma soka kuli muntu wamene kugwesana kupitila!
\v 8 Ngati kwanja yako kapena kwendo yako ikulengesa kugwa, ijube uyitaye. Chawamapo kuti iwe ungene mu umoyo uli ojubika kapena olemala kuchilapo kuti uponyewe mu mulilo wamene siuzima ukali na manja yabili kapena mendo yabili.
\s5
\v 9 Ngati linso yako ikulengesa kuti ugwe, ichose uiponye kutali naiwe. Chawamapo kuti iwe ungene mu moyo na linso imozi kuchilapo kuti uponyewe mu mulilo wamene siuzima na menso yako yonse.
\s5
\v 10 Onesesa kuti siusula kamwana kali konse. Chifukwa niku uzani kuti ku mwamba ba ngelo babo bama yangana pa nkope ya ba Tate Banga bamene bali kumwamba.
\v 11 Ma buku yakudala yolemekezeka maningi yalibe aya mau yamene yakamba kuti, "Chifukwa Mwana wa Muntu anabwela kupulumusa chia chamene chinasoba."
\s5
\v 12 Muganizapo bwanji? Ngati muntu ali onse ali na nkosa zokwanila handredi, imozi ikataikapo, samasiya zija zamene zili nainte-naini pa mbali pa chulu naku yenda kukasakila ija yamene yataika?
\v 13 Ngati aipeza, zoona nikuuzani kuti, azakondwela maningi pali iyi kuchila pali zija zamene zili nainte-naini zamene sizenze zataika.
\v 14 Chimozi-mozi, sichifunilo cha ba Tate banu bamene bali kumwamba kuti ali onse pali aba bana bangóno aonongeke.
\s5
\v 15 "Ngati mubale wako akulakwila iwe, enda umuzibise cholakwa chake, pakati kaimwe babili chabe. Ngati amvela, iwe wamu bweza mubale wako.
\v 16 Koma ngati akana kukumvela iwe, tengako umozi kapena babili boenda nabo kuli eve kuti kupitila mu kamwa ka mboni zibili kapena zitatu liu ili yonse isimikiziwe.
\s5
\v 17 Ngati akana kubamvelela na beve, zibisa baku mupingo. Ngati akana futi kubamvelela baku mupingo, mulekeni uyu muntu ankale monga wa kunja na wamu sonko.
\s5
\v 18 Zoona nikuuzani imwe, vintu vili vonse vamene mumanga pa ziko viza mangiwa kumwamba, na chili chonse chamene muza mangusula pa ziko chizamangusuliwa kumwamba.
\v 19 Nafuti niku uzani imwe kuti, ngati bantu babili mwagwilizana pa ziko pali chintu chili chonse chamene imwe mupempa, muzapasiwa na ba Tate Banga bamene bali mumwamba.
\v 20 Chifukwa pamene bantu babili kapena batatu bakumana muzina yanga, ine nimapezekapo pakati pabo."
\s5
\v 21 Pamene apo Petul anabwela naku kamba kuli Yesu kuti, "Ambuye, mubale wanga afunika kunilakwila kangati naine kuti nimukululukile? Mpaka kali seveni?"
\v 22 Yesu anamuyanka kuti, "Ine sinizaku uza kuti kali seveni chabe, koma mpaka ma seveni yali kumi yali nkale seveni.
\s5
\v 23 Mwa ichi ufumu wa kumwamba uli monga mfumu wina wamene anali kufuna kuti aoneselane za malonda naba ntchito bake.
\v 24 Pamene bana yamba kupendelana, wantchito umozi banamuleta wamene anali na nkongole zokwanila ndalama ma teni sauzande.
\v 25 Koma chifukwa chakuti sanali nayo njila yolipililamo nkongole iyi, bwana wake analamula kuti agulisiwe, pamozi na mukazi wake na bana bake na vonse vamene anali navo, kuti nkongole ilipiliwe.
\s5
\v 26 Pamene apo wantchito uja anagwa pansi, kugwada pamenso pake, nakukamba kuti, 'Bwana, nipaseniko ntawi, nizalipila zonse nkongole.'
\v 27 Uja bwana wa uja wantchito, chifukwa anamvela chifundo, anamu lekelela naku mukululukila ija nkongole.
\s5
\v 28 Koma uja wantchito ana enda nakupeza umozi wantchito munzake, wamene anali na nkongole zake, zokwanila handeledi. Anamugwila, kumukamata pa mukosi, naku muuza kuti, 'Nilipile nkongole yanga.'
\v 29 Koma wantchito muzake uja anagwa pansi naku mupempa, kukamba kuti, 'Nipaseko ntawi, nizakulipila.'
\s5
\v 30 Koma uja wantchito oyamba anakana. Koma, anaenda naku mupeleka mu ndende mpaka chabe akalipile nkongole zonse zake.
\v 31 Pamene bantchito benangu banzake banaona chamene chinachitika, banakalipa. Banaenda naku uza bwana wabo vonse vamene vinachitika.
\s5
\v 32 "Pamene paja bwana wa uja wantchito anamuitana naku muuza kuti, 'iwe wantchito oipa, naku kululukila nkongole zone chifukwa chakuti wenze wanipempa.
\v 33 Nanga iwe bwanji sunamuchitile chifundo wantchito muzako, monga mwamene ine nenze nakumvelela chifundo?'
\s5
\v 34 Bwana wake anakalipa nakumupeleka kuli bomuzunza mpaka pamene azakakwanilisila kulipila nkongole zake zonse.
\v 35 Nichimozi-mozi mwamene ba Tate banga bazachitila kuli imwe ngati imwe pansi pa mutima wanu simu kululukila mubale wanu.
\s5
\c 19
\cl Mutu 19
\p
\v 1 Pamene Yesu anabwela pambuyo posiliza kukamba aya mau, anachokako ku Galileya nakuyenda kumalo ya Yudeya malo yamene yali kupitilila mumana wa Yodani.
\v 2 Magulu yabantu yanamukonka, anabapolesa kwamene kuja.
\s5
\v 3 Ba Falisi banabwela kuli eve, kumuyesa, kumuuza kuti, "Nanga nichovomelesewa kuti mwamuna asiye mukazi wake palibe chifukwa chili chonse?"
\v 4 Yesu anabayanka kuti, "Nanga kansi simunabelenge kuti wamene anabalenga kuchokela kuchiyambi anabalenga mwamuna na mukazi?
\s5
\v 5 Eve wamene anabalenga anakamba nafuti kuti, 'chifukwa chake mwamuna azasiya tate wake na mai wake kuyenda kukankala pamozi na mukazi wake, aba babili bazankala tupi imozi.'
\v 6 Chifukwa chake sibantu babili manje koma tupi imozi. Chifukwa chake lekani chamene Mulungu aika pamozi, osavomeleza ali onse kuti apatule."
\s5
\v 7 Banakamba kuli eve kuti, "Nanga nichani kansi chamene Mose anatiuza kuti tikazipasa chipepala chosiliza chikwati nakumupisha mukazi?"
\v 8 Anayanka kuti, "Chifukwa cha kulimba mutima kwanu, ndiye chamene Mose anakuvomelezani kuti musiye bakazi banu, koma kuchokela pachiyambi sichinali njila iyi.
\v 9 Nikuuzani imwe, ali onse wamene asiya mukazi wake, kuchoselako chifukwa cha uchiwelewele, ayenda akwatila na mukazi winangu, achita chigololo; nauja mwamuna wamene akwatila uja mukazi osiyiwa achita chigololo."
\s5
\v 10 Bopunzila banamuuza Yesu kuti, "Kansi ngati ndiye mwamene chilili pali mwamuna na mukazi wake, sichintu chabwino kukwatila."
\v 11 Koma Yesu anabayanka kuti, "Sibonse bantu bamene bangavomele chipunziso ichi, koma baja bamene bavomelesewa kuti bachivomele.
\v 12 Chifukwa kuli baja bamene sibafuna chikwatila kuchokela kubadwa kwabo, futi kuli baja bamene sibafuna chikwatila chifukwa cha malamulo yabantu, nafuti kuli baja bamene sibafuna chikwatila chifukwa cha ufumu wa kumwamba. Wamene akwanisa kuchilandila ichi chipunziso, mulekeni achilandile.
\s5
\v 13 Banaleta bana bangóno kuti aba ikepo kwanja nakuba pempelela, koma bopunzila bake banabakalipila.
\v 14 Koma Yesu anabauza kuti, "Bavomeleseni bana bangóno, osabalesa kuti babwele kuli ine, chifukwa ufumu wakumwamba niwa bantu monga aba."
\v 15 Anaika manja yake pali bana baja, nakuyenda kuchoka kumalo kuja.
\s5
\v 16 Onani, muntu anabwela kuli Yesu nakukamba kuti, "Apunzisi, nichintu chiti chabwino chamene ine nifunikila kuchita kuti nipasiwe moyo wamene siusila?"
\v 17 Yesu anamuyanka kuti, "Nanga nichani kansi chamene iwe unifunsila kuti chabwino nichiti? Pali chabe umozi wabwino, koma ngati ufuna kuti ungene mumoyo, sunga malamulo."
\s5
\v 18 Muntu uja anayanka kuti, "Yati malamulo?" Yesu anayanka kuti, "Osapaye, usachita chigololo, usabe, usankale kamboni waboza,
\v 19 lemekeza batate bako na bamai bako, ukonde muzako monga mwamene uzikondela iwe weka."
\s5
\v 20 Uja mwamuna anamuyanka kuti, "Vonse ine nimachita. Nanga kwasala chani chamene nifunika kuchita?"
\v 21 Yesu anamuyanka kuti, "Ngati ufuna kuti unkale ofikapo, yenda, kagulise vonse vamene ulinavo, upase bosauka, ndipo uzankala na chuma kumwamba; ubwele, unikonke."
\v 22 Koma pamene munyamata uyu anamvela vamene Yesu anamuuza, anaenda omvesana chifundo, chifukwa anali olemela maningi.
\s5
\v 23 Yesu anauza bopnzila bake kuti, "Zoona nikuuzani imwe, nichintu chovuta kuti muntu olemela angene mu ufumu wakumwamba.
\v 24 Nafuti nikuuzani kuti, nichintu chapafupi kuti Kavalo ingene muka muboó ka nyeleti kuchila kuti muntu olemela angene mu ufumu wa Mulungu."
\s5
\v 25 Pamene bopunzila bake banamvela ichi, banali banadabwa kwambili nakukamba kuti, "Kansi nanga nindani wamene angapulumusiwe?"
\v 26 Yesu anabalangana nakukamba kuti, "Kuli bantu ichi nichintu chamene sichingakwanilisike, koma kuli Mulungu vintu vonse vikwanilisika."
\v 27 Pamene apo Petulo anayanka kuti, "Onani, tinasiya vintu vonse naku kukonkani. Nanga ise tizapezamo chani?"
\s5
\v 28 Yesu anabauza kuti, "Zoona nikuuzani imwe, mu mubadwe pamene Mwana wa Muntu azakankala pa mupando wake waulemelelo, naimwe bamene munanikonka muzakankala pa mipando zachifumu zili 12, kuweluza mitundu kumi na zibili zaku Israeli.
\s5
\v 29 Ali wonse wamene anasiya manyumba, ba bale, balongo, batate bake, bamai bake, bana, kapena munda chifukwa cha zina yanga azakalandila kupitililapo ntawi zili 100 na kulandila moyo wamene siusila.
\v 30 Koma bambili wamene bali boyambilila bazankala bosilizila, na baja bosilizila bazankala boyambilila.
\s5
\c 20
\cl Mutu 20
\p
\v 1 Ufumu wakumwamba uli monga mwine wa munda wamene kuseni-seni anaenda kungenesa bantchito kuti basebenzele mumunda wake wa ma gilepsi.
\v 2 Pamene ana mvelana nabo bantchito kubalipila ndalama imozi pa siku, anabatuma kuyenda kukasebenza mumunda wake wa mpesa.
\s5
\v 3 Ana enda nafuti kuma fili koloko yamu mazulo nakupeza benangu bantchito bali imilile pamalo yamalonda.
\v 4 Anabauza kuti, "Naimwe endani mukasebenze mumunda wanga wa mpesa, yamene nizaona kuti ndiye malipilo yanu yabwino ndiye yamene nizakupasani.' Pamene apo bana enda kukasebenza.
\s5
\v 5 Anabwela aendako futi pa ntawi ya twelofu koloko na fili koloko ntawi ya muzuba, nakuchita chimozi-mozi.
\v 6 Kamozi futi pantawi ya leveni koloko anaenda nakupeza futi bantu benangu bali imilile banalibe vochita. Anabauza kuti, 'Nanga nichani imwe mwaimilila apa kulibe vamene mungachite?'
\v 7 Banamuyanka kuti, 'Chifukwa kulibe wamene atingenesa ntchito ise.' Anabauza kuti, 'Kansi naimwe endani mu munda wanga mukasebenze.'
\s5
\v 8 Pamene inafika ntawi yakumazulo, mwine wa munda uja anauza omulanganila munda kuti, 'Baitane bantchito ubapase ndalama zabo.'
\v 9 "Pamene bantchito baja bamene banangenesewa ntchito pa ntawi ya levini koloko banabwela, ali onse analandila ndalama imozi.
\v 10 Pamene bantchito baja bamene banayambilila kungena ntchito banabwela, banaganizila kuti beve bazalandila ndalama zambili, koma na beve banalandila ndalama imozi chabe.
\s5
\v 11 Pamene banalandila malipilo yabo, banadandaula pali mwine wa munda uja.
\v 12 Banakamba kuti, 'Aba bantchito babwela ntawi yokomboka basebenza chabe ola imozi, koma mwaba folesa chimozi-mozi naise, bamene tasebenza ntchto yolimba yalelo na kupya kwa zuba.'
\s5
\v 13 "Koma mwine wa munda uja anayanka nakukamba kuti, 'Muzanga iwe, ine sininakulakwile. Nanga sitenze tamvelana iwe naine kuti muzafola ndalama imozi?
\v 14 Ani tenga ndalama yamene iyi ndiye malipilo yako uyende nakuyenda. Ine nasanka kuti na aba bamene bangena ntchito posililiza kuti bafole chimozi-mozi naiwe.
\s5
\v 15 Nanga kansi sinilinazo mpavu zochita vilivonse na katundu wanga? Kapena uchita nsanje chifukwa cha mutima wanga opasa?
\v 16 Chifukwa cha ichi uja muntu osilizila azankala oyamba, uja oyamba ndiye azankala osilizila." Ma buku yochilapo yakudala maningi yalibe aya mau yamene yakamba kuti, "Bambili baitaniwa, koma nibangóno bamene basankiwa."
\s5
\v 17 Pamene Yesu anali kuyenda ku Yelusalemu, anatenga bopunzila bake bali kumi na babili pambali, munjila muja nakubauza kuti,
\v 18 "Onani, apa tiyenda ku Yelusalemu, kwamene Mwana wa Muntu azapelekewa kuli bakulu ba nsembe na bolemba. Bazamuweluza kuti apaiwe
\v 19 na kumupeleka kuli bantu Bakunja kuti bamunyoze, bamukwapule, naku mupachika pamutanda. Koma pa siku yachitatu azakaukisiwa."
\s5
\v 20 Pamene apo mai wa bana ba Zebediya anabwela na bana bake bamuna. Anagwada pansi pali eve naku pempa chintu.
\v 21 Yesu anamuyanka kuti, "Nanga nichani chamene mufuna?" Ana yanka kuti, "Vomelezani kuti bana banga babili aba bakankale, umozi kukwanja yanu yaku manja na wina kukwanja yanu yaku manzele, mu ufumu wanu."
\s5
\v 22 Koma Yesu anamuyanka nakukamba uti, "Suziba chamene upempa iwe. Nanga ungakwanise kumwa gome yamene ine nifuna kumwa apa?" Banamuyanka, "Tingakwanise."
\v 23 Anabayanka kuti, "Gome yanga eeeh muzamwa. Koma kunkala ku kwanja yanga ya kwanja na kwanja yanga ya manzele sichintu chakuti ine ningalamule, koma nikwa baja bamene banabakonzela kuli ba Tate banga."
\v 24 Pamene baja bopunzila benangu bali kumi banamvela ichi, banakalipa maningi pali aba babale babili.
\s5
\v 25 Koma Yesu anabaitana kuti babwele kuli eve naku bauza kuti, "Imwe muziba kuti basogoleli ba bantu Bakunja bamabafuna kulangiza kuti ndiye basogoleli ku bantu babo, nabaja bantu bozibika bapamwamba bamalangiza mpavu zabo pali beve.
\v 26 Koma kuli imwe visankale njila iyi. Koma, uja muntu wamene afuna kunkala mukulu pali imwe ayenela ankale wantchito kuli imwe,
\v 27 nauja wamene afuna kuti ankale oyamba pakati panu imwe lekani ankale wantchito kuli imwe,
\v 28 monga mwamene Mwana wa Muntu eve sanabwelele kuti bantu bamutumikile, koma kuti atumikile, nakupeleka umoyo wake kunkala cho-ombolelako bantu bambili."
\s5
\v 29 Pamene banali kuyena kuchoka ku Yeliko, gulu ikulu inamukonka.
\v 30 Panali ba mpofu babili bamene banali nkale mumbali mwa museu. Pamene banamvela kuti Yesu apita, banapunda kukamba kuti, "Ambuye, Mwana wa Davide, timvelelenikoni chifundo."
\v 31 Koma gulu inabakalipila, kubauza kuti bankale chabe ziii, koma beve banapunda mokwezekelatu mau, "Ambuye, Mwana wa Davide, timvelelenikoni chifundo ise."
\s5
\v 32 Yesu anaimilila nakubaitana kukamba kuti, "Nanga nichichani chamene imwe mufuna kuti ine nikuchitiline?"
\v 33 Banamuyanka kuti, "Ambuye, tifuna kuti menso yatu yayambe kuona."
\v 34 Pamene apo Yesu, mogwiliwa nachifundo, anagwila mu menso mwabo. Pamene apo banayamba kuona naku mukonka Yesu.
\s5
\c 21
\cl Mutu 21
\p
\v 1 Pamene Yesu na bopunzila bake bana fika pafupi na Yelusalemu kumalo ya Betipagi, ku pili ya Oliva, Yesu anatuma bopunzila bake babili,
\v 2 kubauza kuti, "Endani mu munzi wamene uli pasogolo, pamene mungena muzapeza ka bulu komangilila, naka mwana kake pamozi. Mutu mangusule mutulete kuli ine.
\v 3 Ngati muntu ali onse akufunsani poni pali twemve, imwe mukambe kuti, 'Ambuye ndiye bamene batufuna,' uja muntu azakulekani kuti mututenge mubwele nato."
\s5
\v 4 Manje chamene ichi chinachitika kuti vintu vamene anakamba muneneli vikwanilisike. Anakamba kuti,
\v 5 "Mu uzeni mwana mukazi waku Ziyoni kuti, 'Ona, Mfumu yako ibwela kuli iwe, Yozichepesa yakwela bulu-pa kamwana ka bulu, ka mwana ka nyama yonyamula katundu'"
\s5
\v 6 Pamene apo bopunzila banayenda naku chita monga mwamene Yesu anabauzila.
\v 7 Banaleta bulu naka mwana ka bulu naku ikapo vovala vabo pali vemve, na Yesu anankala pa vovala.
\v 8 Bambili mu gulu banayanzika vovala vabo pa museu, na benangu bana juba tumitengo naku tuika pa museu.
\s5
\v 9 Pamene apo ma gulu ya bantu yana enda pasogolo pa Yesu na baja bamene banali kumukonka uku ndishi bapunda kukamba kuti, "Hosana kuli mwana wa Davide! Niodalisika wamene abwela muzina ya Ambuye! Hosana kumwamba!"
\v 10 Pamene Yesu anangena mu Yelusalemu, muzinda one unagwedeseka naku kamba kuti, "Kansi nindani uyu?"
\v 11 Magulu yanayanka naku kamba kuti, "Uyundiye Yesu muneneli wamene achokela ku Galileya."
\s5
\v 12 Yesu anangena mu tempele. Anapisha bonse bamene banali kugulisa naku gula mu tempele, naku pindamula ma tebulo yabaja bochinjisa ndalama na yabaja bamene banali kugulisa nkunda.
\v 13 Anabauza kuti, '"Chinalembewa kuti, 'Nyumba Yanga izaitaniwa kuti ni nyumba yama pempelo,'koma imwe mwaipanga kunkala nyumba yaba kawalala."
\v 14 Pamene apo kunabwela ba mpofu na bolemala mu tempele, anabapolesa.
\s5
\v 15 Koma pamene ba bakulu-bakulu nsembe na bolemba bna ona vintu vabwino vamene analikuchita, napamene bana mvela bana bangóno-bangóno mu tempele banali kupunda naku kamba kuti, "Hosana kuli Mwana wa Davide," banakalipa maningi.
\v 16 Banamuuza kuti, "Nanga umvela vamene bakamba?" Yesu anabayanka kuti, "Eeeh! Nanga simunabelenge kuti, 'Kuchokela mukamwa mwa bana bangóno na bana bamene banyonka imwe mwakonza matamando'?"
\v 17 Pamene apo Yesu anabasiya nakuyenda kuchoka mumuzinda nakuyenda ku Betani kwamene anagona.
\s5
\v 18 Manje kuseni-seni pamene anabwelela ku muzinda, anamvela njala.
\v 19 Anaona mutengo wa mukuyu mumbali mwa museu, anaenda kuli mutengo uyu naku peka kuti munali chabe ma tepo. Anau uza mutengo uyu kuti, "Musakankalemo chipaso chilichonse muli iwe futi," na pamene apo uja mutengo unayuma.
\s5
\v 20 Pamene bopunzila banaona ichi, bana dabwa nakukamba kuti, "Nanga nichani uyu mutengo wayuma pamene apa?"
\v 21 Yesu anabayanka nakukamba kuti, "Zoona niku uzani imwe kuti, ngati muli na chikulupilo nafuti simukaikila, imwe simuzachita chabe chamene chachitika kuli uyu mutengo wa mukuyu, koma imwe muzakamba na kuli iyi pili kuti, 'Tengewa uyende ukaponyewe mu nyanje,' chamene icho chizachitika.
\v 22 Chili chonse chamene imwe mupempa mu pempelo, mokulupilila, muzalandila."
\s5
\v 23 Pamene Yesu anafika mu tempele, bakulu-bakulu bansembe na bakulu-bakulu ba bantu banabwela kuli eve pamene anali kupunzisa naku kamba kuti, "Nanga nimpavu zabwanji zamene iwe usebenezesa kuchita ivi, nindani wamene anakupasa mpavu zamene izo?"
\v 24 Yesu anabayanka naku kamba kuti, "Naimwe ine nizakufunsani funso imozi. Ngati muzaniyanka, naine nzaku uzani mpavu zamene ine nisebenzesa kuchita ivi vintu.
\s5
\v 25 Kubatiza kwa Yohane-kunachokela kuti? Kumwamba kapena ku bantu?" Banakambisana beka-beka, nakukamba kuti, "Apa ngati takamba kuti, 'Kunachokela kumwamba,' eve azati uza kuti, 'Nanga nichani kansi chamene imwe simuna mukulupilile eve?
\v 26 Koma ngati takamba kuti, 'Ku bantu,' tiyopa gulu, chifukwa bonse bama ona Yohane kunkala muneneli."
\v 27 Banamuyanka Yesu kuti, "Ise sitiziba." Na eve ana bayanka kuti, "Naine sinizaku uzani mpavu zamene ine nisebenzesa kuchita ivi vintu.
\s5
\v 28 Nanga imwe muganizapo chani apa? Muntu anali na bana babili. Ana enda kuli uja oyamba naku muuza kuti, 'Mwana wanga, enda ukasebenze mu munda lel.'
\v 29 Uyu mwana anayanka kuti, 'Ine siniza enda,' koma anabwela achinja mutima naku yenda kukasebenza.
\v 30 "Uja muntu anabwela ayenda kuli mwana wake wokonkapo naku muuza chimozi-mozi. Eve anayanka nakukamba kuti, 'Niza enda, atate,' koma sana ende.
\s5
\v 31 Ni uti pali aba babili wamene anachita chamene ba tate babo banali kufuna?" Bana yanka kuti, "Uja oyamba." Yesu anabauza kuti, "Zoona niku uzani imwe kuti, baja bamusonko na bachiwelewele bazayambilila kungena mu ufumu wa Mulungu imwe mukalibe kungena.
\v 32 Chifukwa Yohane anabwela kuli mwe minjla yolungama, koma imwe simunamukulupilile. Koma baja bamusonko na bachiwelewele banamu kulupilila. Koma imwe, na pamene imwe muna ona ivi, simuna tembenuke kuti mumukulupilile.
\s5
\v 33 "Mvelani mwambo wina. Kunali muntu, mwine wa munda. Anashanga mpesa, naku ikako chochingilizila, anakumba kotwela mpesa uja, na kumanga nyumba ya olonda, naku ibwelekesa pa ndalama kuli bolima mpesa. Anaenda ku ziko ina.
\v 34 Pamene ntawi yo kolola inafika, anatuma bantchito bake kuli balimi ba mpesa kuti batengeko mbali yake ya mpesa.
\s5
\v 35 Koma baja bolima mpesa bana batenga bantchito bake, bana menyapo umozi, bana payapo umozi, naku tema myala wina.
\v 36 Futi, uja mwine anatuma benangu bantchito bake, bambili bochila baja boyambilila, koma baja balimi ba mpesa bana bachita chimozi-mozi.
\v 37 Kuchoka apa, mwine anatuma mwana wake kuli beve, kukamba kuti, 'Mwana wanga bazamuyopa.'
\s5
\v 38 "Koma pamene baja balimi ba mpesa banaona mwana uja, banakambisana kuti, 'Uyu ndiye azakasala na chuma.' Bwelani, tiyeni timupaye titenge chuma chake.'
\v 39 Banamutenga, banamutaya mu munda wa mpesa naku mupaya.
\s5
\v 40 Manje pamene mwine wa munda azakabwela, azakabachita chani baja balimi ba mpesa?"
\v 41 Banamu yanka kuti, "Azaba ononga momvesa chifundo baja bantu boipa munjila yau kali maningi, azabwela abwelekese munda wake kuli benangu balimi ba mpesa, bantu bamene bazamu pasa mbali yake ya vokolola pa ntawi yo enela."
\s5
\v 42 Yesu anabauza kuti, "Nanga imwe simuna belenge mumalemba kuti, 'Mwala wamene baja bomanga bana kana wankala ndiye ogwila nyumba yonse. Ichi chinachokela kuli Ambuye, ndipo nichabwino mumenso yatu'?
\s5
\v 43 Chifukwa chake nikamba kuli imwe kuti, ufumu wa Mulungu uzapokewa kuli imwe naku pasiwa kuli ziko yamene izabala vipaso vake.
\v 44 Ali onse wamene agwelapo pali uyu mwala azapwanyiwa kunkala tumyala tuongóno tungóno. Koma pali ali onse wamene uzagwela aza onongeka."
\s5
\v 45 Pamene bakulu-bakulu ba nsembe na ba Falisi bana mvela izi myambo, banaziba kuti anali kukamba pali beve.
\v 46 Banali kufuna kuti bamugwile, koma banali kuyopa gulu ya bantu, chifukwa bantu banali kumu kamba kuti ni muneneli.
\s5
\c 22
\cl Mutu 22
\p
\v 1 Yesu ananena kwaiwo kachibili mumyambi, ndikunena,
\v 2 ''Ufumu wakumwamba uli monga mfumu inakonzekela pwando yachikwati wa mwana wake mwamuna.
\v 3 Anatuma banchinto bake kuitana bonse bamene banaitaniwa kupwando yachikwati ichi, komanso sibanabwele.
\s5
\v 4 Nafuti mfumu inaitana banchito bake, nakuti, ' Uzani baja woitaniwa, '' Onani, nakonzeka mugonelo wanga. Ng'ombe yanga natubana twake toina vapaiwa, ndiponso izi zonse nizokonzewa. Bwelani kupwando yaukwati.''
\s5
\v 5 Koma sianafakileko nzelu ndiponso anayenda, alibonse kuulimi wake, ndiponso wina kumalonda yake.
\v 6 Benangu banagwila banchito bamfumu, ndiponso anamvesewa nsoni, nakubapaya.
\v 7 Mfumu inakalipa na kutuma basilikali bake, ndiponso banapaya baja bopaya na kushoka muzinda yawo.
\s5
\v 8 Ndipo anauza banchito bake kuti, 'Chikwati nichokonzekela, koma baja bamene banaitaniwa sibanali oyenela.
\v 9 Mwaichi yendani pokumanilana njila ndi kuitana banthu bambili bamene mungakwanise kuitana kupwando yachikwati monga mwamene mungapezele.'
\v 10 Banchito banayenda munjila, na kusonkanisa banthu pamozi bonse bamene banapeza, woipa na babwino. Na mumalo yokwatililamo chikwati yanazula na balendo.
\s5
\v 11 Koma pamene mfumu inabwela mukati kuona balendo, Inaona mwamuna wamene sanavale zovala vaukwati.
\v 12 Mfumu inamuuza kuti, ' Munzanga, wabwela bwanji kuno ulibe vovala vaukwati?' Koma uja mwamuna analibe mau.
\s5
\v 13 Koma mfumu inauza banchito kuti, ' Mumangeni mwamuna uyu kumanja na mendo, ndipo mumutaile panja pofipa, pamene pazankhala kulila nakusheta meno.'
\v 14 Koma banthu bambili nioitaniwa, koma wosankhidwa nibang'ono.''
\s5
\v 15 Ndipo bafalisi banayenda na kukonzekela mwamene bangamugwilile Yesu mumakambidwe yake.
\v 16 Ndipo banatuma kuli eve bophunzila bake, pamozi nama Herodiya. Banamuuza Yesu kuti, '' Muphunzisi, tiziba kuti ndiwe wazoona, na kupunzisa njila za Mulungu. Siumasamalila maganizo ya aliyense, ndipo siulangiza kusanka pa banthu.
\v 17 Koma tiuze, uganizapo bwanji? kodi nichovomelezewa kupasa musonko kuli kaisala kapena iyai?''
\s5
\v 18 Koma Yesu anaziba kuipa kwawo na kukamba kuti, '' Nichifukwa chani chamene muniyesela, imwe bachinyengo?
\v 19 Nilangizeni ndalama zamisonko.'' Ndipo banabwelesa kobili kuli eve.
\s5
\v 20 Yesu anakamba kuli beve, '' Nanga vili muchifanizilo na zina yabandani ivi? ''
\v 21 Yesu anabauza kuti, '' kaisala.'' Ndipo Yesu anabauza kuti, '' Kansi pasani kuli kaisa zinthu zamene zili za kaisala, ndipo kuli Mulungu zamene zili za Mulungu.''
\v 22 Pamene banamvela ivi, banadabwisiwa. koma anamusiya ndikuchokapo ndipo banayenda
\s5
\v 23 Pali ija siku masadusi benangu, bananena kuti kulibe chisinsimuso, anabwela kuli iye. Anamufunsa iye,
\v 24 Nakunena, '' Aphunzisi, Mose ananena, ' ngati munthu afa, kopanda mwana, mubale wake afunika kukwatila mukaziwake na kumubalilako mubale wake.
\s5
\v 25 Kunali babale bali 7. Oyamba anakwatila na kumwalila. Kosasiyapo mwana aliyense, Anasiya mukazi wake kuli mubale wake.
\v 26 Ndipo mubale wake anachita chimodzimodzi, koma wachitatu, nakufikila kufikila naku mubale wa namba 7.
\v 27 Kuchokela kwa aba onse, mukazi anafa.
\v 28 Manje pakuukisiwa azankhala mukazi wandani pali aba babale bali 7? chifukwa onse anamukwatilapo mukazi uyu.''
\s5
\v 29 Koma Yesu anayanka ndiponso ananena kwaiwo, ''Ndimwe osoba, Chifukwa simuziba malemba olo mphamvu za Mulungu.
\v 30 Koma pachisinsimuso sibamakwatila olo kupasiwa kuchikwati. Koma, ankhala monga angelo kumwamba.
\s5
\v 31 Koma kulinganiza nazakuukisidwa kwa akufa, simunabelenge zamene zinanenewa kwainu ndi Mulungu, nakunena,
\v 32 ' Kuti ndine Mulungu wa Abulahamu, ndiponso Mulungu wa Isaki, ndiponso Mulungu wa Yakobu'? Mulungu si Mulungu wa akufa, '' Koma ni Mulungu wa amoyo.''
\v 33 Pamene magulu inamvela izi, anadabwisiwa ndi kapunzhisidwe kake.
\s5
\v 34 Koma pamene afalisi anamvela kuti Yesu abazizilika asadusi, anazikumaniza pamodzi iwo oka.
\v 35 Wina waiwo, okambilako, anamufunsa funso, nakumuyesa_
\v 36 '' Aphunzisi, ni liti lamulo lalikulu pamalamulo?''
\s5
\v 37 Yesu ananena kwaiwo, '' Konda Mulungu wako namutima wako onse, namoyo wako onse, ndiponso ndi nzelu zako zonse.''
\v 38 Iyi ndiye lamulo ikulu yoyamba.
\s5
\v 39 Ndiponso lamulo lacibili lili kuti_ ' Konda ozungulila iwe monga mwamene uzikondela.'
\v 40 Pali aya malamulo yabili ndiye pamene yonse malamulo ndiponso aneneli ziimilila.''
\s5
\v 41 Koma pamene afalisi analipamodzi, Yesu anafunsa funso.
\v 42 Ananena kuti, '' uganiza chani pali za khristu? Kodi ni mwana wandani?'' Ananena kwa iye, '' Ni mwana wa Davidi.''
\s5
\v 43 Yesu ananena kwaiwo, '' Chilibwanji, pamene Davidi alimumuzimu pamene amuitana Ambuye, nakunena,
\v 44 Ambuye ananena kuli Mulungu wanga, '' Nkhala kuzanja lamanja, kufikila napanthawi yamene nizapanga adani ako kunkala pamapazi yako.''
\s5
\v 45 Ngati David amaitana kristhu 'Kuti Ambuye,' Angankhale bwanji mwana wa Davidi?
\v 46 Kulibe wamene enze kukwanisa kumuyankha liwu ndiponso kulibe Munthu anayesa kumufunsa mafunso nafuti kuchokela siku ija.
\s5
\c 23
\cl Mutu 23
\p
\v 1 Pamene apo Yesu anakamba kuuza magulu ya bantu na bopunzila bake.
\v 2 Anakamba kuti, "Bolemba na ba Falisi bankala mumupando wa Mose.
\v 3 Chifukwa chake imwe mufunika kumvelela vonse vamene bakuuzani kuti chitani, imwe vichiteni nakuvikonka. Koma musakonke vochita vabo, chifukwa beve bamakamba ivi vintu koma sibamavichita.
\s5
\v 4 Zo-ona chabe, bamamangilila katundu bolema wamene niwovuta kuunyamula, bamau ika pama pewa ya bantu. Koma beve sibangayese kutandizila nangu naka kumo kamozi chabe kuti banyamuleko.
\v 5 Bamachita ntchito yabo kuti bantu babaone. Bamapangisa tuma bokosi toikamo mau ya Mulungu tukulu, nakukulisa vovala vabo kuti baonese monga balemekeza mulungu.
\s5
\v 6 Bamakonda yaja malo yolemekezeka pa pwando na malo ya ulemu muma Sinagogo,
\v 7 na moni bapadela pamalo yamalonda, nakuitaniwa kuti 'Apunzisi' na bantu.
\s5
\v 8 Koma imwe musaitaniwe kuti Ápunzisi,' chifukwa imwe muli na mupunzisi umozi chabe, imwe monse ndimwe babale.
\v 9 Ndipo musaitane muntu ali onse pa ziko kuti batate, chifukwa imwe muli chabe na ba Tate bamozi, bamene bali kumwamba.
\v 10 Musaitaniwe kuti 'mupunzisi,' chifukwa muli chabe na opunzisa umozi, Kristu.
\s5
\v 11 Koma uja wamene ndiye mukulu pakati panu ankale wantchito.
\v 12 Ali onse wamene azitukumula aza chepesewa, na uja wamene azichepesa azakwezewa.
\s5
\v 13 Koma soka kuli imwe, bolemba na imwe ba Falisi, bantu baboza! Mumavala ufumu waku mwamba pa menso pa bantu kuti basangenemo. Imwe bamene futi simungenamo, futi simuvomeleza baja bamene bafuna kuti bangenemo kuti bangene.
\v 14 Ma lemba yolemekezeka maningi yakudala yalibe aya mau yali mu verse ya nambala 14 (Koma yenangu yamaika iyi vesi pasogolo pa vesi 12).
\v 15 "Soka kuli imwe, bolemba na ba Falisi, imwe ba mankalidwe yaboza! Chifukwa mumadya muma nyumba ya bazimai bofelewa, mumachita ichi pamene mupempela pempelo itali yakuti imwe muonekele. Chifukwa cha ichi imwe muzalandila kuweluziwa kukulu." Soka kwa imwe, bolemba naimwe ba Falisi, bantu ba mankalidwe yaboza! Muma enda kujumpa nyanja na minda kuti mukatembenule muntu umozi, pamene atembenuka uyo muntu, mumamulenga kunkala kochilapo kabili mwana waku moto monga mwamene mulili imwe.
\s5
\v 16 'Soka kuli imwe, basogoleli bamene balibe menso, imwe bamene mumakamba kuti, 'Wamene alapa kulapila pa tempele, ichi chilibe ntchito. Koma uja wamene alapila pali golide yamene ili mukati mwa tempele iyi, eve amangiwa na kulapa kwake.'
\v 17 Imwe basogoleli bopusa bamene balibe menso! Nanga nichiti chikulu, golide kapena tempele yamene ilengesa golide kunkala yoyela?
\s5
\v 18 Na, 'alionse wamene alapila pa guwa, palibe kantu. Koma uja wamene alapila pali chopeleka chamene chilipo, amangiwa na kulapa kwake.'
\v 19 Imwe ba mpofu! Nanga nichiti chikulu, chopeleka kapena guwa yamene ilengesa chopeleka kunkala choyela?'
\s5
\v 20 Chifukwa chake, uja wamene alapila pa guwa alapila na vonse vamene vilipo.
\v 21 Uja wamene alapila pa tempele alapila pali yeve na uja wamene ankalamo mukati mwake.
\v 22 Na uja wamene alapila kumwamba alapila pamozi na mupando wamfumu wa Mulungu na wamene ankalapo.
\s5
\v 23 Soka kuli imwe, bolemba naba Falisi, bantu ba munkalidwe waboza! Imwe mumapeleka chakumi pali vintu voika kuvakudya, monga sabola, dili na kamini, koma mwasiya vintu vamene vili volema mumalamulo-kuweluza na chifuno na chikulupililo. Koma ivi asembe mumachita mosasiya vija vinangu vosachitiwa.
\v 24 Imwe basogoleli ba mpofu, bamene muma kwinyilila pali ka inzi koma muma mela kavalo!
\s5
\v 25 "Soka kuli imwe, bolemba na ba Falisi, bamunkalidwe waboza! Chifukwa mumasuka chabe kunja kwa gome nakwa mbale, koma mukati ndimwe bozula na kuzikonda na kuzikondwelesa.
\v 26 Imwe ba mpofu ba Falisi! Sukani poyamba mukati mwa gome na mbale, kuti nakunja kungankale kwabwino nakwemve.
\s5
\v 27 "Soka kuli imwe, bolemba naimwe ba Falisi, bamunkalidwe waboza! Chifukwa imwe muli monga choika pa manda, chamene kunja chioneka nichabwino, koma mukati mwake ndimwe bozula na mafupa ya bantu na vonse vintu voipa.
\v 28 Chimozi-mozi, kunja muoneka monga ndimwe bantu bolungama kuli bantu, koma mukati ndimwe bozula na munkalidwe oipa na kusakonka ma lamulo.
\s5
\v 29 "Soka kuli imwe, bolemba na ba Falisi, bamunkalidwe waboza! Imwe muma manga manda ya ba neneli naku konza bwino manda ya bantu banali bachilungamo.
\v 30 Mukamba kuti, 'Asembe tinaliko ntawi yama kolo yatu, asembe sitinatengeko mbali muku paya ba neneli.'
\v 31 Chifukwa chake imwe mupeleka umboni kuzi weluza pamweka kuti imwe ndimwe bana ba bantu baja bamene banapaya baneneli.
\s5
\v 32 Imwe muzulisilatu vamene visasiyako batate banu.
\v 33 Imwe njoka, imwe bana ba nsato, nanga muzakwanisa bwanji kutaba kuweluza kwa ku mulilo?
\s5
\v 34 Chifukwa chake, nikutumilani baneneli na bantu banzelu na bolemba. Benangu pali aba muzaba paya naku ba pachika, benangu muzaba menya muma sinagogo yanu nakuba pilikisha kuchoka mumuzinda uyu kuyenda mumzinda winangu.
\v 35 Malipilo yake niyakuti pali imwe pazabwela magazi yonse ya chilungamo yamene yanatikiwa paziko, kuyambila magazi ya Abelo, kufikila magazi ya Zakaliya mwana wa Balakiya, wamene muna paya pakati pa malo oyela na guwa.
\v 36 Zoona nikuuzani kuti, ivi vintu vonse vizabwela pali uyu mubadwe.
\s5
\v 37 "Yelusalemu, Yelusalemu, iwe wamene upaya baneneli nakutema myala baja bamene batumiwa kuli iwe! Nikangati kamene ine nafuna kuti ni ike pamozi bana bako, monga mwamene nkuku imaikila pamozi bana bake pansi pama papiko yake, koma iwe siunali kufuna!
\v 38 Ona, nyumba yako yakusalila yoónongeka.
\v 39 Chifukwa nikuuza iwe kuti, iwe siuzakaniona nafuti kufikila pa ntawi yamene iwe uzakakamba kuti niodalisika wamene abwela muzina ya Ambuye."'
\s5
\c 24
\cl Mutu 24
\p
\v 1 Yesu anachoka mu tempele kauyenda njila yake. Bopunzila bake banabwela kuli eve naku mulangiza ma mangidwe ya tempele.
\v 2 Koma anabayanka nakubauza kuti, "Nanga simuviona ivi vonse? Zoona niku uzani kuti, kulibe nangu mwala umozi wamene uzasala pamwamba pa wina wamene siuza pwanyika.
\s5
\v 3 Pamene anankala pa Pili ya Oliva, bopunzila bake banabwela kuli eve pa beka naku kamba kuti, "Tiuzeni, niliti pamene ivi vintu vizakachitika? Nanga cholangiza kubwela kwanu nichani na cha kusila kwa mubadwe?"
\v 4 Yesu anayanka nakukamba kuti, "Nkalani bochenjela kuti muntu ali onse asakutaiseni.
\v 5 Chifukwa bantu bambili bazakabwela muzina yanga. Bazakakamba kuti, 'Ine ndine Kristu,' bazakataisa bantu bambili.
\s5
\v 6 Muzakamvela nkondo na nkani ya nkondo. Onani kuti imwe musavutike, chifukwa ivi vintu viyenela kuchitika; koma kusila kwa ziko sikunafike.
\v 7 Chifukwa ziko izakaimila ziko ina, ufumu ufumu wina. Kuzankala njala na kungambika kwa ziko mumalo yosiya-siyana.
\v 8 Koma ivi vintu vonse nikuyamba chabe kwa kubaba kwa mumimba yakubeleka.
\s5
\v 9 Chokonkapo bazakakupelekani ku mavuto naku kupayani. Muzaka zondewa na maiko yonse chifukwa cha zina yanga.
\v 10 Kukonkapo kwake bambili bazagwa, naku gulisana wina na munzake naku zondana.
\v 11 Baneneli bambili bazakaima naku taisa bantu bambili.
\s5
\v 12 Chifukwa chakuti kupyanya lamulo kuza enda pasogolo, chikondi cha bambili chizaka zizila.
\v 13 Koma uja wamene alimbikila mpaka kosilizila azapulumuka.
\v 14 Utenga wabwino wa ufumu uzalalikiwa konse paziko yapansi kunkala mboni kuli maiko yonse. Vokonkapo nikusila kwa ntawi.
\s5
\v 15 "Mwa ichi, imwe mukaona chintu chochitisa nyansa chamene chilengesa kutaya chiyembekekezo, chamene chinakambiwa na muneneli Daniyeli, chili imilile mu malo yoyela" (obelenga amvesese),
\v 16 "baja bamene bali mu Yudeya lekani batabile kuma pili,
\v 17 uja wamene ali pa malata ya nyumba asa seluke kuti atengemo kali konse mu nyumba,
\v 18 nauja wamene ali mumunda asabwelele kuti akatenge chovala chake.
\s5
\v 19 Koma soka kuli baja bamene bali na bana mu masiku yaja!
\v 20 Mupempele kuti kutaba kwanu kusakankale mu ntawi ya mpepo kapena pa Sabata.
\v 21 Chifukwa kuzakankala kuvutisiwa kukulu, kuchililatu mwamene kunalili kuchokela pamene ziko inayambila mpaka lelo, kapena kuti vizakachitikako futi iyayi.
\v 22 Asembe aya ma siku siyanachepesewe, kulibe wamene angapulumuke. Koma chifukwa cha baja bolungama aya masiku yaza chepesewa.
\s5
\v 23 Ngati muntu ali onse aku uzani kuti, 'Onani, uyu apa Kristu!' kapena, 'Uyo kristu!'musakulupilile.
\v 24 Chifukwa ba Kristu baboza na baneneli baboza bazakabwela naku langiza volangiza vikulu na vodabwisa, kuti bataye, ngati nichokwanilisika, nabaja bolungama.
\v 25 Onani, naku uzani pamene kukali ntawi.
\s5
\v 26 Chifukwa cha ichi, ngati baku uzani kuti, 'Onani, ali mu chipululu,' imwe osayendako ku chipululu. Kapena, 'Onani, ali mu chipinda chamukati,' imwe osakululupilila.
\v 27 Mwamene kaleza kaya yakila kuchokela ku mawa kuonekela naku mazulo, ndiye mwamene kuzakankalila kubwela kwa Mwana wa Muntu.
\v 28 Kwamene kuli nyama yakufa, ndiye kwamene kuzankala vikwangala.
\s5
\v 29 "Koma pamene kuvutikiswa kuzasila zuba izaka nkala bii, mwezi siuzakapasa ku unika kwake, nyenyezi zizakagwa kuchokela kumwamba, na mpavu zaku mwamba zizaka gwedezeka.
\s5
\v 30 Apa manje ndiye pamene kuzakaonekela cho onesela Mwana wa Muntu kumwamba, na mitundu zonse za pa ziko zizaka lila. Bazakamuona Mwana wa Muntu abwela pa makumbi yaku mwamba mwa mpavu na ulemelelo wa ukulu.
\v 31 Azaka tuma bangeli bake na kulila maningi kwa lipenga, bazaka ika pamozi balungami bake kuchokela ku mpepo zinai, kuyambila kumbali imozi ya kumwamba mpaka kufikila mbali ina.
\s5
\v 32 "Tenganiponi punzilo pali mutengo wa mukuyu. Pamene paja pamene ntambi yake inkala yoteka nakumela matepo, imwe muziba kuti ntawi ya zuba ili pafupi.
\v 33 Chimozi-mozi, pamene imwe muzakaona ivi vintu vonse, muyenekela kuziba kuti ali pafupi, ali pa chiseko.
\s5
\v 34 Zoona niku uzani iwe, uyu mubadwe siuzakapita mpaka ivi vintu vonse vikachitike.
\v 35 Kumwamba na pansi ponse pazakapita, koma mau yanga siyazakapita.
\s5
\v 36 Koma kukamba pali siku kapena ntawi kulibe wamene aziba, na bangelo bonse pamozi mali kumwamba, na Mwana, koma ba Tate.
\s5
\v 37 Monga mwamene yanalili masiku ya Nowa, chimozi-mozi mwamene kuzankalila kubwela kwa Mwana wa Muntu.
\v 38 Monga mwamene masiku yanalili chikalibe kufika chigumula bantu banali kudya na kumwa, kukwatila na kupelekewa kuchikwati kufikila pamene Nowa anangena mu bwato,
\v 39 sibanazibe kantu kali konse mpaka pamene chigumula chinabwela naku batenga-chimozi-mozi mwamene kuzankalila kubwela kwa Mwana wa Muntu.
\s5
\v 40 Bamuna babili bazankala mumunda-umozi azatengewa, winangu azasiyiwa.
\v 41 Bakazi babili bazankala bakutwa na chotwela-umozi azatengewa, winangu azasiyiwa.
\v 42 Chifukwa chake, nkalani bochenjela, chifukwa imwe simuziba siku yamene Ambuye banu bazabwela.
\s5
\v 43 Koma imwe muzibe ichi, kuti asembe uja mwine wa nyumba anaziba ntawi ya usiku yamene kawalala azabwela, asembe anankala olangana kuonesesa kuti nyumba yake isangenelewe.
\v 44 Chifukwa chake imwe mufunikila kunkala bokonzekela, chifukwa Mwana wa Muntu azaka bwela pa ntawi yamene imwe simuyembekezela.
\s5
\v 45 "Nanga ni uti wamene ndiye okulupililika wamene ba bwana bake baika kulanganila nyumba yabo kuti abapase va kudya pa ntawi yo enela?
\v 46 Odalisika ni uja wantchito wamene pamene bwana wake abwela azamupeza akali kuchita ntchito.
\v 47 Zoona nikuuzani kuti bwana uja azamu ika bwana pali chuma chake chamene ali nacho.
\s5
\v 48 Koma ngati wantchito oipa akamba mumutima wake kuti, 'Bwana wanga achedwa kubwela,'
\v 49 ayamba naku menya bantchito banzake, naku mwa nakudya pamozi naba chakolwa,
\v 50 uja bwana wake azakabwela pa siku yamene eve saganizila napa ntawi yamene eve saziba.
\v 51 Bwana wake azakamu juba mu vigaba vigaba naku mupasa malo pamozi nabaja bantu bama nkalidwe yaboza, kwamene kuzankala kulila naku sheta meno.
\s5
\c 25
\cl Mutu 25
\p
\v 1 "Ufumu wakumwamba uzakankala monga ba namwali bali kumi bamene banatenga tunyali twabo kuyenda kuti bakakumane naye okwatiliwa.
\v 2 Basanu pali aba banali bopusa koma basanu benangu banali bochenjela.
\v 3 Chifukwa pamene banamwali bopusa banatenga tunyali twabo, sibanatenge na mafuta yosebenzesa mu tu nyali twabo.
\v 4 Koma banamwali bochenjela bana tenga tu gubu pamozi na tunyali twabo.
\s5
\v 5 Manje pamene okwatiliwa anachedwa kufika, bamvela tulo naku gona.
\v 6 Koma pa kati ka usiku kunali kupunda, 'Onani, okwatiliwa! Endani muka kumane na e.
\s5
\v 7 Pamene apo bonse baja banamwali banaima naku yasha tu nyali twabo.
\v 8 Baja bopusa bana uza bochenjela kuti, 'tipempako mafuta chifukwa tunyali twatu tuzazima.'
\v 9 "Koma baja bochenjela banayanka kuti, 'Chifukwa siku zankala yokwanila kuti imwe naise tigabane, imwe endani kuli baja bamene bagulisa mukagule yanu yosebenzesa.'
\s5
\v 10 Pamene bana enda kukagula, okwatiliwa anabwela, na bonse baja bamene banali bokonzekela bana enda na-e kupwando, bana koma nachiseko.
\v 11 "Kuchoka apa manje baja banamwali benangu banabwela nakukamba kuti, 'Bwana, bwana, tisegulileni koni.'
\v 12 "Koma anabayanka nakukamba kuti, 'Zoona nikuuzani imwe, ine sinikuzibani imwe.'
\v 13 Onesesani, chifukwa imwe simuziba siku kapena ntawi.
\s5
\v 14 "Chifukwa chili monga muntu wamene afuna kuenda kuziko ina. Anabaitana bantchito bake naku bapasa chuma chake.
\v 15 Kuli umozi anapasa ndalama zisanu, kuli wina zibili, na kuli wina anapasa ndalama imozi. Ali onse analandila zokwanila monga mwamene angakwanilisile, na uja muntu ana enda pa ulendo wake.
\v 16 Uja wamene analandila ndalama zisanu ana enda pamene apo naku zisebenzesa ndalama zija naku pangilapo ndalama zinangu zokwanila zisanu.
\s5
\v 17 Chimozi-mozi uja wamene analandila ndalama zibili anapangilapo ndalama zinangun zibili.
\v 18 Koma uja wantchito wamen eanalandila ndalama imozi ana enda, naku kumba mugodi, nakubisa ndalama za bwana wake.
\s5
\v 19 Manje pamene panapita ntawi ikulu bwana wa baja bantchito anabwelela naku pendelana ndalama.
\v 20 uja wantchito wamene analandila ndalama zisanu anabwela naku leta ndalama zinangu zisanu. Anakamba kuti, 'Bwana, imwe mwenze munanipasa ndalama zisanu. Onani, ninapangilapo ndalama zinangu zisanu.'
\v 21 "Bwana wake anamu uza kuti, 'Wachita bwino, wantchito wabwino okululupilika! Unali okululupilika pa tuntu tungóno. Apa manje ine nizakupanga o onela vambili. Ngena mu chimwemwe cha bwana wako.'
\s5
\v 22 "Wantchito uja wamene analandila ndalama zibili anabwela nakukamba kuti, 'Bwana, imwe munanipasa ndalama zibili. Onani, napangilapo ndalama zibili zinangu.'
\v 23 Bwana wake anamu uza kuti, 'Wachita bwino, wantchito wabwino okulupililika! Unali okululupilika pali tuntu tungóno. Niza kuika olanganila vintu vambili. Ngena mu chimwemwe cha bwana wako.'
\s5
\v 24 "Pamene apo wanchito uja wamene analandila ndalama imozi anabwela naku kamba kuti, 'Bwana, Niziba kuti imwe ndimwe bolimba mutima. Muma kolola pamene imwe simunashange, ku unjikisa pamene imwe simuna tayepo.
\v 25 Ine ninali na manta, chifukwa chake ine nina enda naku bisa ndalama yanu pansi. Onani, tengani chintu chanu.'
\s5
\v 26 "Koma bwana wake anamu yanka naku muuza kuti, 'Iwe wantchito oipa na ulesi, unaziba kuti ine nima kolola pamene sininashange naku unjikisa pamene sinina tayepo.
\v 27 Iwe asembe una bwelekesa ndalama zanga kuli ba malonda ya ndalama, pakubwela kwanga asembe ninapeza ndalama zanga na za pamwamba.
\s5
\v 28 Tengani ndalama ili kuli eve mupase uja wamene ali na ndalama kumi.
\v 29 Chifukwa muntu ali onse wamene ali nazo, zambili zinangu zizapasiwa-zopitililapo. Koma uli uja wamene alibe kali konse, navija vamene ali navo azapokewa.
\v 30 Mutayeni panja pamene pali mudima uyo wanchito wamene alibe pindu, pamene kuzankala kulila nakusheta meno.'
\s5
\v 31 "Pamene Mwana wa Muntu azabwela mu ulemelelo wake na bangelo bonse pamozi na eve, pamene paja azakankala pa mupando wake waulemelelo.
\v 32 Pa menso pake yonse maiko yazaka kumana, ndipo azakapatulula bantu wina kumuchosa kuli wina, monga mwamene mubusa ama patulula nkosa na mbuzi.
\v 33 Azaika nkosa ku kwanja yake ya kwanja, koma mbuzi zizankala ku kwanja yake ya manzele.
\s5
\v 34 Pamene apo Mfumu azakauza baja bamene bali ku kwanj ayake ya manja, 'Bwelani, imwe bamene munadalisika na ba Tate banga, tengani ufumu wamene banaku konzelani kuchokela pamene ziko inalengewa.
\v 35 Chifukwa ine ninali na njala munanipasa bakudya; ninali na njta munanipasa chakumwa; Ninali mulendo munani landila munyumba zanu;
\v 36 Ninali be vovala imwe munani valika; Ninali odwala imwe munanisamalila; Ninali mu ndende imwe munabwela kuniona.'
\s5
\v 37 "Pamene apo baja bolungama bazakayanka nakukamba kuti, 'Ambuye, niliti pamene ise tinaku onani njala takusapani vakudya? Kapena na njota takupasani chakumwa?
\v 38 Niliti pamene ise tinakuonani mulendo naku kulandilani? Kapena munalibe vovala nakuku valikani?
\v 39 Niliti pamene tinaku onani kuti mudwala kapena mu ndende naku bwela kukuonani?'
\v 40 "Pamene apo Mfumu izakayanka naku kamba kuli beve kuti, 'Zoona niku uzani imwe, chamene imwe muna chitila mungóno pali aba babale banga aba, munachitila ine.'
\s5
\v 41 Aza kamba kuli baja bamene bali kukwanja yake ya manzele, 'Chokani apa, imwe botembelelewa, endani mu mulilo wamene unakonzekelewa mudani na bangelo bake,
\v 42 chifukwa ine ninali na njala, koma simunani pase vakudya; Ninali na njota, koma imwe simunani pase chakumwa;
\v 43 Nenze mulendo, koma imwe simunani landile mu manyumba yanu; ninalibe vovala, koma imwe simunani pase vovala; odwala na mu ndende, koma imwe simunani samalile.'
\s5
\v 44 "Pamene apo baza kayanka nakukamba kuti, 'Ambuye, niliti pamene tenze tinakuonani na njala, kapena na njota, kapena mulendo, kapena osavala, kapena odwala, kapena mundende, ndipo ise siti naku tandizeni?'
\v 45 "Azakayanka naku kamba kuti, 'Zoona nikuuzani imwe, vamene imwe simunachitile kuli mungóno pali umozi waba aba, simunachitile ine.'
\v 46 Aba bazaka yenda muku kaulisiwa kwamene sikusila, koma balungami bazangena mu moyo wamene siusila."
\s5
\c 26
\cl Mutu 26
\p
\v 1 Chinabwela chachitika kuti pamene Yesu anasiliza mau yonse, Ananena ku bophunzila bake,
\v 2 "Muziba kuti kuchokela masiku awiri Pasaka ilikubwela, ndiponso mwana wa munthu azapelekewa mu kupachikiwa.''
\s5
\v 3 Ndipo mukulu wabakulu bansembe nabakulu ba banthu banabwela pamodzi mumalo yaopeleka bansembe, wamene analikuitanidwa zina Kayafasi.
\v 4 Banapangana kuti bamugwire mobisa ndiponso nakumupaya.
\v 5 Chifukwa banalikunena kuti, ''Osati nthawi yaphwando chifukwa pangauke chongo pakati pa banthu.''
\s5
\v 6 Manje Yesu anali ku Betaniya munyumba ya Simoni wa khate,
\v 7 pamene anali anasamila pa tebulo, muzimayi wina anabwera kuli eve na botolo ya mafuta yonunkhira ya mtengo wapatali, ndiponso anayatila pamuthu wake.
\v 8 Koma pamene bophunzila bake banaona ichi, banabwela bakalipa ndikunena kuti, ''Nichifukwa chani ulikuonongela?
\v 9 Sembe mafuta yamene aya yagulisiwa pa mutengo ukulu, ndipo izi ndalama sembe zapasiwa kuosauka.''
\s5
\v 10 Koma Yesu, poziba izi, anakamba kuli beve, ''Nichifukwa chani muvutisila muzimayi uyu?
\v 11 Chifukwa achita chinthu chabwino kuli ine. Mumankhala nabosauka nthawi zonse, Koma simuzankhala naine nthawi zonse.
\s5
\v 12
\v 13 Koma pamene anathira mafuta yonunkhila pa thupi langa, achita izi kukonzeka kufwikiliwa kwanga. Nikuuzani zoona, kulikonse kwamene utenga uzalalikiwa muno muziko, chamene uyu muzimayi achita chizakakambiwapo mukukumbukila uyu muzimayi.''
\s5
\v 14 Ndipo umodzi wa kumi na yabiri palibeve oitaniwa Yudasi Isikarioti, anapita kuli akulu ansembe nakufunsa kuti,
\v 15 ''Kodi nichani chamene muzanipasa ngati namubwelesa kuli imwe?'' Banapima ndalama zokwanila masiliva makumi yatatu.
\v 16 Kuyambira pamene paja banasakila nthawi yabwino yopeleka Yesu kulibeve.
\s5
\v 17 Pa siku yoyamba yaphwando ya mukate yamene ilibe chotupisa bophunzila banabwela kuli Yesu nakunena ati? '' Kodi nikuti kwamene mufuna kuti tikakukonzekele malo yodyelamo pasakha?''
\v 18 Anabauza kuti, "Yendani mumuzinda ku mwamuna wina ndiponso mumuuze kuti, 'Mupunzisi anena kuti, ''Nthawi yanga yafika. Nizasunga pasakha pa nyumba yako pamozi na bophunzila banga.''
\v 19 Bophunzila banachita mwamene Yesu anabauzila, ndiponso banakonza chakudya cha Pasakha.
\s5
\v 20 Pamene chinafika kumazulo, Yesu anankhala pansi na bophunzila bake khumi na yabiri na kudya.
\v 21 Pamene banali kudya, anakamba, ''Nikuuzani zoona imwe kuti umodzi pali imwe azanigulisa.''
\v 22 Banamvesewa chisoni, ndiponso wina wache anayamba kumufunsa eve, ''Nditu ine sindine, Ambuye?''
\s5
\v 23 Anayankha ati, ''Wamene aza ngenesa kwanja kwake pamodzi na ine mubeseni ndiye wamene azanigulisa.
\v 24 Mwana wa Munthu azayenda, monga mwamene chinalembedwa pali eve. Koma soka kuli uja munthu wamene azamugulisa! Chinawama ngati uja munthu sanabadwe.''
\v 25 Yuda, wamene enzo yenera kumugulisa anati, '' Kodi ndine, Muphunzisi?'' Anamuuza ati, '' Wazikambila iwe weka.''
\s5
\v 26 Pamene benze bakalikudya, Yesu anatenga mukhate, nakuudalisa, ndiponso anaigomola. Anapasako bophunzila bake nakukamba ati, ''Tengani, mudye. Iyi ndiye thupi yanga.''
\s5
\v 27 Anatenga kapu nakuyamika, Ndiponso anabapasa na kukamba ati, "Mwani, imwe bonse.
\v 28 Chifukwa uyu ndiye mwazi wanga wachipangano wamene unatikiwa kukhululukila machimo ya bambiri.
\v 29 Koma nikuuzani, Sinizakamwapo futi ku chipatso cha mutengo wampesa, mpaka siku yamene nizakamwa mwasopano na imwe mu ufumu wa Batate banga.''
\s5
\v 30 Pamene banaimba nyimbo, banayenda kuphiri ya Olive.
\v 31 Koma Yesu anati kuli beve, "Imwe bonse muzagwa usiku uno chifukwa chaine, chifukwa chinalembedwa, 'Nizakwapula mubusa ndiponso nkhosa zizamwazikana.'
\v 32 Koma pamene nizauka, nizayenda pasogolo painu mu Galileya.''
\s5
\v 33 Koma Petulo anakamba kuti, ''Chingankhale kuti bonse bagwa chifukwa chaimwe, ine sinizagwapo.''
\v 34 Yesu anati kuli eve, ''Nikuuza zoona kuti, lelo usiku pamene kombwe akalibe nakulila, uzanikana katatu.''
\v 35 Petulo anakamba kuli eve ati, ''Chingankhakele kuti ningafele pamozi naimwe, Sinizakukanani.'' Bonse bophunzila bake banakamba chimodzimodzi.
\s5
\v 36 Koma Yesu anayenda na beve kumalo yoitaniwa Getesemani ndiponso anakamba kubophunzila bake, ''Nkhalani pamenepano, pamene paja apo, pamene niyenda mukupempela.''
\v 37 Anatenga Petulo na bana babili ba Zebedi na eve ndiponso anayamba kunkhala na chisoni na kuvutikiwa mutima.
\v 38 Ndipo anakamba kuli beve ati, ''Moyo wanga wazuliwa na chisoni, chakufa nacho. Nkhalani pamenepano ndiponso yanganilani na ine.''
\s5
\v 39 Anayendanso pang'ono pasogolo, anagwesa nkhope na kupempela. Anakamba ati, ''Tate wanga, ngati nichoteka, lekani iyi kapu inipitilile. Koma, osati kulinganiza nakufuna kwanga, Koma kulinganiza nachifunilo chanu.''
\v 40 Anabwela kubophunzila bake ndiponso anapeza baligone, ndiponso anauza Petulo, ''Nichifukwa chani simunga yanganile na ine ora imodzi?
\v 41 Yanganilani na kupempela kuti musagwele mu mayeso. Muzimu ufuna, koma thupi ni yofokela.''
\s5
\v 42 Anayendanso kachibiri mukupempela. Anakamba kuti, ''Tate wanga, ngati ichi sichinganipilile koma chabe nimwe, chifuniro chanu chichitike.''
\v 43 Anabwelanso nakupeza bakaligone, chifukwa manso yabo yanali yolema.
\v 44 Pamene anabasiyanso, anayenda kupempela ka chitatu, ndikunena mau yamodzimodzi.
\s5
\v 45 Ndipo Yesu anabwela kubophunzila bake na kubauza ati, ''Mukaligone na kupumula? Onani, ora ili pafupi, ndiponso Mwana wa Munthu azagulisiwa mu manja yabochimwa.
\v 46 Nyamukani, tiyeni tiyende. Onani, onigulisa alipafupi.''
\s5
\v 47 Pamene enzeli kukamba, Yudasi wina wao pali kumi na abiri, anabwela. Gulu likulu linabwela na eve kuchokela kubakulu bopeleka bansembe ndiponso bakulu ba banthu. banabwela na malupanga na vopumila.
\v 48 Manje munthu wamene enzoyenekela kugulisa Yesu anabapasa chizibiso, ndikunena kuti, ''Aliyense wamene nizaposha nakutomola, ndiye wamene muzagwira.''
\s5
\v 49 Pameneapo anabwela kuli Yesu na kukamba ati, ''Mulibwanji, Baphunzisi!'' ndiponso anamutomola eve.
\v 50 Yesu ananena kuli iye, ''Muzanga, chita vamene wabwela kuchita.'' Ndipo bana bwela, kufaka manja pali Yesu, ndiponso banamugwila.
\s5
\v 51 Onani, umodzi pali bamene banali na Yesu anatambusula kwanja kwake, nakudonsa panga yake, ndiponso anakwapula kapolo wa akulu opeleka bansembe, ndiponso anajuba kwatu yake.
\v 52 Koma Yesu ananena kuli eve, ''Faka panga mumalo yake, chifukwa aliense wamene apaya na lupanga azafa na lupanga.
\v 53 Kodi uganizila kuti asembe sinaitanile Batate banga, asembe sibanitumila ma gulu ya angelo kupambana zikwi khumi na yabiri?
\v 54 Koma nimunjila yabwanji yamene malemba yazafikilisiwamo, kuti izi zichitike?''
\s5
\v 55 Pali ija nthawi Yesu anauza gulu ati, ''Kodi mwabwela na mapanga na vopumilako nakunitenga monga ndine kawalala? Nenzonkhala lyonse mutempele na kupunzisa, ndiponso simunanimange.
\v 56 Koma ivi vonse vachitika kuti malembo ya aneneri yafikilizike.'' Ndiponso bonse bophunzila banamusiya nakuyenda.
\s5
\v 57 Baja bamene banamugwira Yesu banamupeleka kuli Kayafasi mukulu wa bansembe, kwamene bolemba na bakulu banakumana pamodzi.
\v 58 Koma Petulo anamukonkha mosiyako kamalo kang'ono na nyumba ka mukulu wa bakulu bansembe. Anayenda mukati ndiponso anankhala pansi na bamalonda kuti aone vamene vizachokamo.
\s5
\v 59 Manje mukulu wa opeleka nsembe ndiponso bonse bamukabungwe banali kuyanganila paukamboni waboza onamizila Yesu, kuti bamupayilepo.
\v 60 Sibanapeze aliyense, chingankhale bakhamboni bambiri banabwela pasogolo. Koma pambuyo pake babiri banabwela pasogolo
\v 61 ndiponso banakamba ati, '' Uyu mwamuna anakamba kuti, 'Ningakwanisa kuononga tempele ya Mulungu ndiponso nakuimangana futi muma siku yatatu.''
\s5
\v 62 Mukulu wabopeleka nsembe anayimilila no kamba kuli eve ati, ''Kodi ulibe yankho? Nanga nichani chamene bapasila umboni pali iwe?''
\v 63 Koma Yesu anankala zii. Mukulu wabopeleka bansembe anakamba ati, ''Nakulamilila iwe mwa Mulungu wa moyo, tiuze ngati ndiwe Kristu, Mwana wa Mulungu.''
\v 64 Yesu anamuyanka ati, ''Wakamba ivi wamene iwe. Koma nikuuzani imwe, kuchokela pano muzaona Mwana wa Munthu ankhala kuzanja lamanja la Mphamvu, ndiponso alikubwela pa makumbi ya ku mwamba."
\s5
\v 65 Ndipo mukulu wa bopeleka bansembe anang'amba zovala zake ndi kunena kuti, ''Akamba manyozo! Nichani chamene tikalikusakilila bakamboni? Onani, manje mwamvela manyozo.
\v 66 Muganizapo chani?" Banayankha no kamba ati, ''Ayenekela kufa.''
\s5
\v 67 Koma banabwela bamutunyila mata kumanso ndiponso kumumenya, ndikumukwapula na kanjeza kumanja yake,
\v 68 ndiponso ananena, ''Nenelani kuliise, iwe Kristhu. Nanga ni ndani wamene enze kukukwapula?''
\s5
\v 69 Manje Petulo enze nkhale panja pa malo yanyumba, ndiponso wanchito mukazi anabwela kuli eve nakumuuza ati, ''Naiwe wenzeli na Yesu waku Galileyo.''
\v 70 Koma anakana pasogolo pabo bonse, nokamba, ''Siniziba vameneukambapo.''
\s5
\v 71 Pamene anayenda kunja kwanjila, wanchito wina anamuona ndiponso anauza baja benzepo ati, ''Uyu mwamuna naeve enzeli na Yesu waku Nazareti.''
\v 72 Nafuti anakana ndikulapa, ''Sinimuziba!''
\s5
\v 73 Pamene kunapita ka nthawi kang'ono baja bamene bana imilila pafupi banabwela nakumuuza Petulo ati, ''Zoona ndiwe wina wa amodzi aba, chifukwa makambidwe yako yakugulisa.''
\v 74 Koma anayamba kutembelela na kulapa, ''Sinimuziba uyu munthu,'' ndiponso pameneapo kombwe analila.
\v 75 Petulo anakumbuka mau yamene Yesu anakamba, ''Pamene kombwe akalibe kulila uzanikana katatu.'' Ndiponso anayenda panja na kulila kuipa.
\s5
\c 27
\cl Mutu 27
\p
\v 1 Pamene kunacha, bakulu bakulu bansembe na bakulu bakulu ba bantu bana nkala na maganizo pali Yesu kuti bamu paye.
\v 2 Banamumanga, nakumutenga, naku mupeleka kuli Pilato kazembe.
\s5
\v 3 Pamene Yudasi, wamene anamupeleka, anaona kuti Yesu bana mu weluza kuti apaiwe, ana tembenuka naku bweza zija ndalama za Siliva zokwanila ma kumi yatatu kuli bakulu bakulu bansembe na bakulu ba bantu,
\v 4 naku kamba kuti, "Ine nachimwa chifukwa napeleka magazi yamene yalibe mulandu." Koma abanakamba kuti, "Nanga ise tingenamo bwanji? Ziba zako iwe."
\v 5 Pamene apo eve anataya pansi zija ndalama mu tempele, naku yenda, naku yenda kukazi mangilila.
\s5
\v 6 Bakulu bansembe banatenga zija ndalama naku kamba kuti, "Sichovomelesewa kuti ti ike ndalama mu tumba ya tempele chifukwa izi ni mutengo wa magazi."
\v 7 Banakambisana ichi chintu, nakugula na ndalama izi munda wa opanga mpika kuti yankale manda yoikamo malilo yaba lendo.
\v 8 Chifukwa cha ichi uja munda unaitaniwa kuti, "Munda wa Magazi"mpaka na lelo.
\s5
\v 9 Apa chamene chinakambiwa na Yelemiya muneneli chinafikilisiwa, chokamba kuti, "Banatenga ndalama za Siliva ma kumi yatatu, ndalama za mutengo wamene banamuweluziliwa eve kuli bana ba Izilayeli,
\v 10 nakugula munda wa opanga mpika, monga mwamene Ambuye banani uzila ine."
\s5
\v 11 Manje Yesu anaimilila pamenso pa kazembe, kazembe anamufunsa kuti, "Nanga ndiwe Mfumu ya ba Yuda?" Yesu anamu yanka nakukamba kuti, "Ndiwe wamene ukamba chamene icho."
\v 12 Koma pamene banamupasa mulandu ba kulu bansembe na bakulu ba bantu, sanaba yanke chili chonse.
\v 13 Pilato anamufunsa kuti, "Nanga iwe ndishi siumvela zonse milandu zamene aba bakamba pali iwe?"
\v 14 Koma sanamuyanke ngakale liu imozi, kulengesa kuti kazembe anankala odabwa maningi.
\s5
\v 15 Manje pa pwando kunali mwambo wakuti kazembe anali ku masula wa mundende umozi wamene anali kusankiwa na gulu ya bantu.
\v 16 Pa ntawi ija kunali wamu ndende imozi ovuta maningi zina yake Balaba.
\s5
\v 17 Pamene banakumana pamozi, Pilato ana bauza kuti, "Niuti wamene ine nizaku masulilani imwe? Balaba, kapena Yesu wamene aitaniwa Kristu?"
\v 18 Anaziba kuti banamupeleka Yesu kuli eve chifukwa cha nsanje.
\v 19 Pamene anali nkezi pa mupando woweluzilapo, mukazi wake anatumiza mau kuli eve kuti, "Imwe musankale na chochita nawo uyo muntu wamene alibe mulandu. Chifukwa ine navutika vintu vambili chifukwa cha chiloto chamene ine ninali nacho pali eve."
\s5
\v 20 Manje bakulu bansembe na bakulu ba bantu banalimbikisa gulu kuti ipempelele Balaba, nakuti bamupaye Yesu.
\v 21 Kazembe anaba funsa kuti, "Niuti pali aba babili wamene mufuna niku masulileni imwe?" Banayanka kuti, "Balaba."
\v 22 Pilato anabafunsa kuti, nanga uyu muntu Yesu wamene aitanaiwa kuti Kristu nimuchite chani?" Bonse banayanka kuti, "Mupachikeni."
\s5
\v 23 Pamene apo anakamba kuti, "Chifukwa chani, nimulandu wa bwanji wamene apanga?" Koma banapunda mokweza mau kukamba kuti, "Mupachikeni."
\v 24 Pamene Pilato anaona kuti kulibe chamene angachitepo, koma panayamba kunkala pokoso, anatenga manzi, nakusamba kumanja pa menso pa gulu ya bantu, naku kamba kuti, "Ine nilibe mulandu pali magazi ya uyu muntu wamene alibe mulandu. Onani vamene muzachuta naye imwe."
\s5
\v 25 Bonse bantu banakamba kuti, 'Lekani magazi yake yankale pali ise na bana batu."
\v 26 Pamene apo anamu masula Balaba, koma anamukwapula Yesu naku mupeleka kuti apachikiwe.
\s5
\v 27 Pamene apo basilikali ba uja Kazembe banamuenga Yesu kuenda naye ku Boma ikulu naku bwelesa pamozi gulu yonse yaba silikali.
\v 28 Banamu chosa vovala nakumu valika mukanjo wofila.
\v 29 Banapanga chisote cha ufumu cha minga naku muika pa mutu, naku mupasa ndondo kumanja yake ya kwanja. Banamu gwadila naku munyoza, kukamba kuti, "Tikuoneni, Mfumu ya ba Yuda!"
\s5
\v 30 Banamutunyila mate, naku tenga ndondo naku mumenya pa mutu mobwezelapo.
\v 31 Pamene banasiliza kumunyoza, banamuchosa mukanjo naku muvalika vovala vake, nakumupeleka kuti apachikiwe.
\s5
\v 32 Pamene bachoka, banapeza mwamuna ochokela ku Saileni zina yake Simoni, wamene banakakamiza kuti aende nabo pamozi kuti amunyamulile mutanda.
\v 33 Banabwela ku malo yoitaniwakuti Gologota, yamene itantauza kuti "Malo ya Bonzo yaku mutu."
\v 34 Banamupasa vinyo kuti amwe osankaniziwa na ndulu. Koma pamene anayesa kuti amwe, anakangawa.
\s5
\v 35 Pamene banamupachika, banagabana vovala vake kupitila muku teya njuga,
\v 36 banankala pansi naku mulonda eve.
\v 37 Pamutu wake bana lembapo mulandu wake, wamene unalembeka kuti, "Uyu ndiye Yesu, mfumu yaba Yuda."
\s5
\v 38 Vigabenga vibili vinapachikiliwa pamozi na eve, umozi ku kwanja yake ya manja na wina ku kwanja yake ya manzele.
\v 39 Bantu bamene banali kupita banali kumutukwana, uku bapukunya mutu
\v 40 nakukamba kuti, "Iwe wamene unali kufuna kuononga tempele naku imanga futi mu masiku yatatu, zipulumuse weka! Ngati ndiwe Mwana wa Mulungu, seluka ubwele pansi kuchoka pa mutanda!"
\s5
\v 41 Chimozi-mozi bakulu bakulu bansembe banali kumunyoza, pamozi na bolemba na bakulu-bakulu, kukamba kuti,
\v 42 "Anali kupulumusa benangu, koma eve sakwanisa kuzipulumusa. Eve ndiye Mfumu wa Izilayeli. Mulekeni aseluke abwele pansi pa mutanda, ndiye pamene ise tizamukulupilila.
\s5
\v 43 Akulupilila muli Mulungu, mulekeni Mulungu amupulumuse manje apa, ngati Mulungu avomela kumu masula. Chifukwa ana kamba kuti, 'Ine ndine Mwana wa Mulungu."
\v 44 Chimozi-mozi vigabenga vija vamene vinapachikiwa pamozi na eve vina munyoza.
\s5
\v 45 Manje kuchokela ntawi ya twelve koloko yamu zuba kufikila ntawi ya fili koloko yamu zuba kunankala chimudima pa ziko yonse.
\v 46 Pa ntawi ya 3 koloko yamu zuba, Yesu anapunda na liu yokweza naku kamba kuti, "Eli, ELi, lama sabakatani?" kutantauza kuti, "Mulungu wanga, Mulungu wanga, nichani chamene mwanilekelela ine?"
\v 47 Pamene baja bamene banali imilile banamvela ichi, banakamba kuti, "Aitana Eliya."
\s5
\v 48 Pamene apo umozi pali baja ana enda naku tenga tonje, aizulisa na vinyo vosasa, ai ika pa ndondo ya ntente, nakumupasa kuti amwe.
\v 49 Bonse bamene banasala banakamba kuti, "Musiyeni eka. Lekani tione ngati Eliya azabwela kuti amupulumuse."
\v 50 Pamene apo Yesu analila na liu yokweza naku peleka muzimu wake.
\s5
\v 51 Onani, chinyula chogabisa tempele china ngámbika pakati kuyambila kumwamba kufikila pansi, na ziko inagwedezeka, na myala zina ngámbika.
\v 52 Manda yana seguka, ma tupi ya bantu boyela bamene bana gona yanaukisiwa.
\v 53 Bana choka mu manda pamene eve anaukisiwa, naku ngena mu muzinda oyela, naku onekela kuli bambili.
\s5
\v 54 Manje pamene Kentuliyo pamozi nabaja bamene banali kuona Yesu banaona kungambika kwa ziko na vintu vamene vinachitika, banayopa nakukamba kuti, "Zoona uyu anali Mwana wa Mulungu."
\v 55 Bazimai bambili bamene banakonka Yesu kuchokela ku Galileya kumusamalila banaliko kulanganila patali.
\v 56 Pali aba panali Maria Madalena, Maria mai wake wa Yakobo na Yosefe, na mai wa bana ba Zebediya.
\s5
\v 57 Pamene kunakala mazulo, kunabwela mwamuna olemela ochokela ku Alimatiya, zina yake Yosefe, wamene anali opunzila wa Yesu.
\v 58 Anafika kuli Pilato naku pempa tupi ya Yesu. Pamene apo Pilato anabauza kuti bamupase.
\s5
\v 59 Yosefe anatenga tupi, kui vumbatila mu nyula yo tuba,
\v 60 naku iika mumanda yake yamanje yamene ana kumba mu mwala. Pamene apo anaika chimwala chikulu pa komo ya manda naku enda.
\v 61 Maria Madalena na uja Maria winangu banaliko kuja, banali nkale kulangana manda.
\s5
\v 62 Siku yokonkapo, yamene inali siku yokonka siku Yokonzekela, bakulu-bakulu ba nsembe na ba Falisi banali banakumana pamozi na Pilato.
\v 63 Banakamba kuti, "Bwana, ise tikumbukila kuti uyu muntu waboza pamene anali na moyo, anali anakamba kuti, 'Pakapita masiku yatatu nizauka futi.'
\v 64 Chifukwa cha ichi imwe lamulani kuti manda baya londe kufikila siku ya chitatu, ndaba bopunzila bake bangabwele nakuba tupi yake naku yamba ku uza bantu kuti, 'Auka kubakufa,' na kunamiwa kosilizila kuzankala kukulu kuchilapo paja poyamba."
\s5
\v 65 Pilato anabauza kuti, "Tengani malonda. Endani mukaonesese kuti manda yalondewa munjla mwamene imwe mungakwanilisile."
\v 66 Pamene apo banayenda naku londesa manda, kuvala chimwala naku ikapo bolonda.
\s5
\c 28
\cl Mutu 28
\p
\v 1 Manje paku yenda kusila kwa Sabata, pamene kunayamba kucha siku yo yamba ya Sabata, Maria Madalena na uja Maria wina bana bwela kumanda.
\v 2 Onani, kunali kungambika kwa ziko, chifukwa mungeli wa Mulungu anaseluka kuchokela kumwamba, nakubwela kuchosapo chimwala, naku nkalapo pachimwala.
\s5
\v 3 Anali kuoneka monga kaleza, na vovala vake vinali votuba monga matalala.
\v 4 Bolonda bana njenjema na manta naku nkala monga bantu bakufa.
\s5
\v 5 Mungeli ana kamba nabo bazikazi naku bauza kuti, "Musayope, chifukwa ine niziba kuti musakila Yesu, wamene anapachikiwa.
\v 6 Salipo pano, koma aukisiwa, monga mwamene anakambila. Bwelani muone pa malo pamene Ambuye banagona.
\v 7 Endani mwa musanga muka bauze bopunzila bake kuti, 'Aukisiwa kubakufa. Onani, aenda akusogolelani kuyenda ku Galiyeya. Kwamene kuja muzamuona.' Onani, naku uzani."
\s5
\v 8 Bakazi baja banachokako kumanda mwamusanga na manta mo kondwela kukulu, naku tamanga kuti bakauze bopunzila bake.
\v 9 Onani, Yesu anaba kumana naku bauza kuti, "Moni!" Bazikazi banabwela, nakugwila mendo yake naku mupembeza.
\v 10 Yesu anabauza kuti, "Musankale na manta. Endani mukabauze babale banga kuti bachokeko ku Galileya. Kwamene uja bazaniona."
\s5
\v 11 Manje pamene bakazi banali kuyenda, onani, benangu pali bamalonda bana enda mumuzinda naku uza bakulu-bakulu bansembe vintu vonse vamene vinachitika.
\v 12 Pamene ba nsembe banakumana na bakulu bakulu naku kambisana pali ichi chintu na beve, bana pasa ndalama zambili maning kuli ba silikali
\v 13 naku bauza kuti, "Benangu mubauze kuti, 'Bopunzila ba Yesu benze bana bwela usiku ndishi ise tili gone nakuba tupi yake.'
\s5
\v 14 Ngati iyi nkani yafika kuli ba kazembe, ise tizakamba nabo kuti imwe musa vutike mutima."
\v 15 Mwa ichi baja basilikali bana tenga ndalama naku chita monga mwamene bana bauzila. Iyi nkani ina pelekewa maningi kuli ba Yuda bambili ndipo yapitiliza kufikila mpaka lelo.
\s5
\v 16 Koma baja bopunzila banali kumi na umozi bana enda ku Galileya, ku pili yamene Yesu anabauza.
\v 17 Pamene banamuona, banamupembeza, koma benangu banakaikila.
\s5
\v 18 Yesu anabwela kuli beve naku bauza kuti, "Zonse mpavu zapasiwa kuli ine kumwamba na pansi.
\v 19 Endani imwe muka pange bopunzila mu maiko yonse. Muba batize mu zina ya ba Tate, ya Mwana, na ya Muzimu Oyela.
\s5
\v 20 Mubapunzise kuti bamvele vintu vonse vamene ine nina kuuzani. Onani, Ine nili naimwe ntawi yonse, mpaka kufikila kosilila ntawi."