\v 10 Ndi wokongola bwanji chikondi chako, mlongo wanga, mkwatibwi wanga! Chikondi chako chiposa vinyo motani, ndi fungo labwino la zonunkhira zako kuposa zonunkhiritsa zilizonse. \v 11 Milomo yako, mkwatibwi, ikukha uchi; uchi ndi mkaka zili pansi pa lilime lako; kununkhira kwa zovala zako ndikununkhira kwa Lebano.