\c 3 \v 1 Usiku ndili pabedi langa ndinalakalaka amene moyo wanga umkonda; Ndinamfunafuna, koma sindinamupeze. \v 2 Ndinati kwa ine, "Ndidzuka ndi kupyola pakati pa mzinda, m'misewu ndi m'mabwalo; ndidzafufuza amene moyo wanga umkonda." Ndinamfunafuna koma sindinamupeze.