nya-x-nyanja_1ki_text_reg/08/22.txt

1 line
520 B
Plaintext

\v 22 Solomoni anaimilila pasogolo pa guwa ya bansembe ya Yehova, pamenso pa banthu bonse ba Israyeli, natambasulira manja ake kumwamba. \v 23 Iye anati, "Yehova, Mulungu wa Israeli, palibe Mulungu wina monga imwe kumwamba kapena pansi pano wamene amasunga chipangano chake na bakapolo banu bamene bamayenda pamenso panu na mutima wabo bonse; \v 24 Imwe bamene mwasunga pamozi na mutumiki wanu Davide batate banga, vamene munamulonjeza. Zoona, munakamba na kamwa kanu ndipo mwakanilisa na kwanja kwanu, monga chili lelo.