nya-x-nyanja_1ki_text_reg/14/11.txt

1 line
536 B
Plaintext
Raw Normal View History

\v 11 Aliyense wa Yerobiamu amene adzafera mumzindawo, agalu adzamudya, ndipo aliyense wofera kutchire adzamudya ndi mbalame za mmlengalenga, pakuti ine Yehova ndanena zimenezi. \v 12 Chotero nyamuka, mkazi wa Yerobiamu, bwerera kunyumba kwako; mapazi ako akalowa mmudzi, mwana Abiya adzafa. \v 13 Aisiraeli onse adzamulira ndi kumuika mmanda. Ndi iye yekha wa mbanja la Yerobiamu amene adzalowa mmanda, chifukwa mwa iye yekha, mnyumba ya Yerobiamu, munapezeka chilichonse chokoma pamaso pa Yehova Mulungu wa Isiraeli.